Dømingos Anthony

Dømingos Anthony For I a'm not ashamed of the Gospel

11/09/2024

"Osamalimbana ndi anthu oti alibe bvumbulutso la moyo wanu, penyani kutsogolo osafoka"

11/09/2024

".... ziwanda zikhulupiriranso, ndipo zinthunthumira".-Yakobo 2:19
Yakobo akutsimikiza kuti Ngakhale ziwanda zimakhulupirira kuti Mulungu ndi m'modzi, komanso akuti zimanjenjemera - Koma zosiyana ndi ife nzakuti, ziwandazo sizingapulumuke, Koma tikuona kuti ziwanda zikudziwa kuti Mulungu ndi m'modzi komanso zikunjenjemera.

Chomvetsa chisoni akristu a masiku ano amakaikira zoti kuli Mulungu, ndipo pamaso pa Mulungu amakhala akuchitirapo masewera. Koma taonani, ziwanda zimanjenjemera komanso kuchita mantha ndi Mulungu, kodi ndi chifukwa chani mumachimwa mwadala, kodi si chifukwa chakuti simuopa Mulungu, so mukapambanidwe ndi ziwanda zimene sizingapulumuke?. Akuti zimanjenjemera chifukwa cha mantha, inuyo muzichita pamene mukutchula dzina la Mulungu, muziopa, chifukwa Mulunguyo ndi wamkulu kuposa ife Ngakhale kuposa ziwandazo. Chimo limodzi lomwelomwelo kumangolipanga, anthu kukuthandizani kuti musiye, koma ayi ndithu Chimo lomwelomwelo kulikakamira, chifukwa simunjenjera pamaso pa Mulungu, mpaka kuchita kuposedwa ndi ziwanda - Chonchi mungagonjetse Chiwanda inu?😥

08/09/2024

Musakwatirane ndi mwamuna amene si okhulupiririka kwa Mulungu, pakuti ngati iye si okhulupiririka kwa Mulungu amene anamulenga, kodi chikukupangitsa kuganiza kuti adzakhala okhulupiririka kwa iwe ndi chani?

08/09/2024

Inde mumati Mpingo ulionse uli ndi malamulo ake, koma chimene ndikudziwa ine ndi chakuti baibulo ndi imodzi, tsono let the Bible speak about "Women" in the churches.
According to the Bible, si kololedwa Kuti mkazi aphunzitse mwamuna, si kololedwa Kuti mkazi aime kutsogolo mumpingo kapena kuguwa mkumaphunzitsa koma pamene amuna ali momwemo, ndipo kunena kwa mtumwi Paulo akuti ichi ndi chochititsa manyazi. Ndikufuna muone lero kuti anthu ambiri amene amanena kuti amaopa mau a Mulungu sikuti amaopadi, ndipo zinthu zina amazilakwira mwadala.

1 AKORINTO 14:34-35 "Akazi akhale chete m'Mipingo. Pakuti sikuloledwa kwa iwo kulankhula. Koma akhale omvera, monganso chilamulo chinena,... pakuti kunyazitsa mkazi kulankhula mu Mpingo".

Sikutinso ndingachite kupempha inu kuti Kodi vesiyi ikunena chani ayi, because this vesi is very clearly, kuyambira nthawi imene Mpingo unayamba, Ngakhale anthu olemba mbiri ya zochitika, mpaka nthawi ya kumangidwa pamodzi kwa Bible, sitiona akazi akumalalikira, sitiona akazi akukhala azibusa, mkazi alibe ulamuliro womaphunzitsa mumpingo. Ndipo Paulo yemweyo akuuza timoteo kuti "1 Timoteo 2:11-12 Mkazi aphunzire akhale wachete m'kumvera konse. Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale chete". Muwerenge mpaka vesi 15.
Paulo mtumwi sakuletsa kuti mkazi aphunzire, koma akuletsa kuti mkazi aphunzitse mwamuna or amuna. But you can see now, mpaka kunja kuno kuli azibusa aakazi, amene amaphunzitsa mmipingo yawo. Si zochokera m'baibulo kuti mkazi akhale m'busa wa Mpingo wa Mulungu Amene anaugula ndi Mwazi wake. Zinazitu ndi zotsatira za kusamvera. Ndikufuna ndikuuzeni kuti anthu amene amamvetsa baibulo kapena amene amakhala ofuna kumvera Mulungu sagwa ulesi kuchita mau a Mulungu olembedwawa mu chipangano chatsopano. Mudzapulumuka bwanji ngati kuyambira pano mau a Mulungu akukutsutsani?. Ndipo ndi tsoka amene amatsutsa choonadi chotere, pakuti akudzionetsera poyera kuti ali against Mulungu.

07/09/2024

"Nthawi ija munkasalako kudya, koma pano munasiiratu, kumbukirani pamene munagwera ndipo mulape".😢

05/09/2024

As long as you keep God first in your life, you’ll forever be blessed.🙏🙏🛐🕊️

05/09/2024

"Zochitachita zanu zimakupangitsani kukhala patali ndi Mulungu, make sure kuti pamene mukupemphera mukusunga chiyero"

05/09/2024

"Munthu ukakhala pamaso pa Mulungu, Ngakhale adani ako apemphere bwanji kuti ugwe, iwe sudzagwa mu dzina la Yesu Kristu"

05/09/2024

"Munthu ndiwe mkristu, chifukwa cha zovuta Zina m'moyo uno, mkupezeka kuti wadzimangirira wafa, Kodi Mulungu akakulandira? Why?"

04/09/2024

Osamatsegulira Aliyense mtima wanu, enatu amangofuna kulowamo kuti akubereni kenako atulukemo nakusiyeni m'mavuto.

04/09/2024

NTHAWI 😢
Tisamalire nthawi, chifukwa Masiku ano ndi oipa, tisaononge nthawi yathu pa kuchita zoipa, tiyeni tigwiritse bwino ntchito nthawi, pa ola Lina lililonse anthu amakhala akumwalira, ndipo pa ola lililonse anthu amakhala akuchita ngozi, tsono ngati chilipo chabwino chimene tikuyenera kuchita, tiyeni tichitiretu, ngati mkuthandiza winawake, tiyeni titero, ngati mkupemphera, tiyeni Tipempheretu tidakali ndi moyo, chifukwa nthawi imadutsa mwachangu. Tiyeni tigwiritse ntchito nthawi yathu pa kucuitira umboni za Yesu Kristu, kulalikira Uthenga wabwino.

"TSOGOLO LANU" 🙁                       "Maso ako ayang'ane m'tsogolo,  zikope zako zipenye moongoka"_ Miyambo 4:25Moyo u...
03/09/2024

"TSOGOLO LANU" 🙁
"Maso ako ayang'ane m'tsogolo,
zikope zako zipenye moongoka"_ Miyambo 4:25
Moyo uno ndi ulendo, ulendo wake ndi wautali, ndipo ena amagwa, amafa paulendou, ena amakafika. Wolemba buku la Miyambo ati maso ako ayang'ane m'tsogolo, Nthawi zina timatha kuchita zinthu mosalingalira za m'mene zinthuzo zikukhudzira Tsogolo lathu, kotero timatha kuononga Tsogolo labwinobwino lija.
Dziwani kuti chifukwa cha adani obisika ena amabwera ngati abwenzi, mapemphero awo amakhala akuti mukhale muli ovutika choncho mpaka imfa, ndipo chifukwa chakuti iwo amakhala amodzi opanga kuti zinthu zisatheke, zinthu zimakhala zikuvutadi. You can see Ambiri mu ulendou amagwamo, ena kudzakhala chinthu chimene sankayembekeza atakhala, kuseli kwa kuvuta kwa nyengo kuli zinthu zothandizira kuti mukhalebe choncho, sometimes mizimu yoipa imakumanga kuti moyo wako usasinthe, ndipo umakhala otemberereka. ..zikope zako zipenye moongoka, Musagone muuzimu, khalani openya, ndipo pempherani kosalekeza, pakuti ndi MULUNGU yekha amene akhoza kumasulira matcheni onse a mdiyerekezi, ndi Mwazi wa Yesu Kristu umene ukhoza kukutsukani ndi kukuchotsani ku matemberero ndi kukhala oyera, ndipo Palibe Chiwanda Ngakhale chimzimu choipa chimene chikhoza kusewerera pamaso pa inu. Lero gwadani pemphererani Tsogolo lanu kuti Mulungu akhale mtsogoleri wanu mu ulendou uwu.
🙏🏼

02/09/2024

"Pamene moyo wako ukupita chitsogolo, adani amachuluka, chifukwa Ngakhale abale ako omwe amakondwera akakuona ukuvutika"🙁

02/09/2024

"Nthawi zambiri ena mwa anthu Amene amakuda, amakhala akumva kuwawa ndi moyo wako chifukwa akudziwa za chimene udzakhala"

30/08/2024

Ndiye pali mipingo imene umachita kulipira ndalama kuti Ubatizidwe😏

26/08/2024

ZOFOKETSA MUUTUMIKI .......
Mu utumiki wautali, utumiki wa kulalikira Uthenga wabwino wa Ambuye wathu Yesu Kristu, zilipo zochitika zambiri zimene zimagwetsera m'mbuyo anthu Ambiri. Ndipo Chifukwa cha ichi sakhala olimba mu utumiki wawo.

1. KUNYOZEDWA
- Nthawi zambiri kunja kuno kuli anthu onyoza, Amene amakunyoza Ngakhale ulalikire bwanji, ndipo Ambiri mwa iwo amakhala anthu opemphera, so inu nonse olalikira mau a Mulungu osamaopa Ngakhale kuchita manyazi kaamba koti winawake akukunyozani, keep up, pakuti Uthenga womweo umene ena akuunyoza, ndi umene winawake akuumva bwino ndipo moyo wake wauzimu wasintha.

2. KUSAYAMIKA
-Kusayamika ndi khalidwe imodzi mwa makhalidwe a anthu m'masiku otsiriza ano, alipo anthu oti olo mutalemba zomveka bwanji, koma kwa iwo si kanthu, kwao kumakhala kunyoza ndipo kuyamikira amaona ngati mkukutchukitsa. Tsono chifukwa cha kusayamika kwawo osamafooka pakuti kuyamikira kwakukulu kumachokera kwa Mulungu. Tangoyamba ntchitoyi ndipo Mulungu adzakondwera nawe, ndipo ngati unaiyamba kale usafooke, pitiriza.

3. KUDUKIDWA
-Alipo anthu ena amene samakufunira zabwino, ndipo samva bwino akakuona uli kutsogolo kuti ulalikire, ndipo pakakhala pa social media pano akangoona post yako yauthenga amamva mtima kuwawa, ndipo makoment awo amangokhala a attack basi, ("Ukufuna ukhale ngati ndani?", Kodi ndiwe wekha amene umadziwa?", Palibe chimene ungatiuze, usawanamize anthu iwe,?") Amalankhula izi ndi mtima wodukidwa, mtima wanjiru. Usataye nawo Nthawi anthu amenewo. Tadutsamo ndipo talimba nazo, kutinyoza mkungodzitengera temberero kusanjika pa temberero linzache.

Anyamata anzanga, zilipo zambiri zimene anthu amatha kupanga kuti alimbane nawe, ndangofuna kukuuzani izi zokha, koma osafooka, pitirizani kulalikira Uthenga wabwino.
Domingos Anthony
Ngati zilipo zoonjezera, lembani 👇 Comment.

25/08/2024

Kod ndizoyenela monga banja Mamuna ndi mkaz kumapemphera mpingo osiyana

23/08/2024

"Ngakhale kuti anthu akude bwanji, sangafufute ulosi umene Mulungu anaika mwa iwe okhudza chimene udzakhala"

22/08/2024

"Chosangalatsa m'chakuti, Mulungu akati inde, umakhala inde, ndipo akati ayi, umakhala ayi, Tsogolo lanu Mulungu yekha ali dziwa"

Endereço

Tete

Website

Notificações

Seja o primeiro a receber as novidades e deixe-nos enviar-lhe um email quando Dømingos Anthony publica notícias e promoções. O seu endereço de email não será utilizado para qualquer outro propósito, e pode cancelar a subscrição a qualquer momento.

Entre Em Contato Com O Negócio

Envie uma mensagem para Dømingos Anthony:

Vídeos

Compartilhar

Empresas De Mídia nas proximidades


Outra Produtor de vídeo em Tete

Mostrar Todos