Nkhoma Synod Radio

Nkhoma Synod Radio Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Nkhoma Synod Radio, Broadcasting & media production company, Lilongwe.
(1)

Nkhoma Synod Radio is a christian Radio station under the C.C.A.P Nkhoma Synod, which intends to bring people closer to God using well produced Christian Programs

 Lero pa 2 October ndi tsiku limene m'busa Masona Kaluluma Tembo wa mu mpingo wa CCAP Nkhoma Synod amakumbukira tsiku la...
02/10/2025



Lero pa 2 October ndi tsiku limene m'busa Masona Kaluluma Tembo wa mu mpingo wa CCAP Nkhoma Synod amakumbukira tsiku lakubadwa kwawo.

Tiyeni tiwafunire zabwino Abusa a Tembo pamene akukondwerera tsiku lakubadwali.

 Yemwe wasankhidwa kukhala phungu wa nyumba ya malamulo ku dera la pakati m'boma la Nkhotakota a Sylvester Ayuba James a...
02/10/2025



Yemwe wasankhidwa kukhala phungu wa nyumba ya malamulo ku dera la pakati m'boma la Nkhotakota a Sylvester Ayuba James ati ali ndi lingaliro lotengera ku nyumba ya malamulo bill yofuna kusintha zaka zomwe mtsogoleri wa dziko ndi aphungu amakhalira pa mpando.

Iye wati akufuna kuti nyumbayi idzakambirane kuti mtsogoleri wa dziko komanso aphungu-wa adzikhala pa mpando zaka 7 kapena 8 pasanachitike chisankho china.

Iye wati kuchititsa zisankho pa zaka zisanu zilizonse ndi chimodzi mwa zinthu zomwe zimaononga chuma cha dziko lino.

Pakadali pano mtsogoleri wa dziko ndi aphungu amakhala pa mpando zaka zisanu pasanachitikenso chisankho.

: Promise Thom

 Bungwe lomenyera ufulu wa anthu la CDEDI m'mawa uno likuyembekezeka kuchititsa msonkhawo wa atolankhani.Mkulu wa bungwe...
02/10/2025



Bungwe lomenyera ufulu wa anthu la CDEDI m'mawa uno likuyembekezeka kuchititsa msonkhawo wa atolankhani.

Mkulu wa bungweli a Sylvester Namiwa ndi womwe akuyembekezeka kutsogolera msonkhawowu.

Msonkhano ukuyembekeza kuyamba nthawi ya 9:30.

  Timu ya Barcelona yakuthidwa ndi timu ya Paris Saint Germin (PSG) usiku wa dzulo mu ligi ya Champions pa bwalo la zama...
02/10/2025




Timu ya Barcelona yakuthidwa ndi timu ya Paris Saint Germin (PSG) usiku wa dzulo mu ligi ya Champions pa bwalo la zamasewro la Estadi Olimpic Lluis Companys.

Barcelona yomwe inali pa khomo inapezera chigoli mwachangu pa mphindi 19 kudzera mwa Ferrani Torres.

Senny Mayulu anawafananitsa masewerawa pa mphindi 38 atagoletsera timu ya PSG kuwasiya masewerowa pa 1-1.

Chigawo cha chiwiri cha masewerowa matimu awiriwa anapanikizana pomwe amakwanitsa kulowerana mzigawo ndikumaphulitsa mizinga ya mabuleti pa golo.

Koma zinayang’ana ku ngolo ku mbali ya Barcelona pomwe timu ya PSG inapezanso chigoli china pa mphimdi 90 kudzera mwakatswiri Goncalo Ramos kuti masewerowa athere 1-2.

Masewera ena a ligi atha motere:

Arsenal 2 – Olympiacos 0
Monaco 2 – Manchester City 2
Dortmund 4 – Bilbao 1
Leverkusen 1 – Eindhoven 1
Union Gilloise 0 – Newcastle United 4
Qarabag 2 – Copenhagen 0
Napoli 2 – Sporting Lisbon 1
Vallarreal 2 – Juventus 2

02/10/2025

MAWU ODZUKIRA

Masalimo 103:2

"Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, ndipo usaiwale zabwino zake zonse."

Ana a Mulungu, tiyeni timuthokoze Ambuye pa zonse zomwe amatichira pa miyoyo yathu.

 Bungwe loyang'ananira malonda a mbewu ya fodya la To***co Commission (TC) lati pofika pa 30 September fodya okwana ma k...
01/10/2025



Bungwe loyang'ananira malonda a mbewu ya fodya la To***co Commission (TC) lati pofika pa 30 September fodya okwana ma kilogalamu 214.2milion wagulidwa ndi ndalama pafupifupi 532.4 milion za kunja.

Malingana ndi mneneli wa bungweli Telephorus Chigwenembe fodyayu wagulidwa ndi mtengo wa pakatikati pa 2.49 za ndalama zakunja.

Mwazina iye wati msika wa fodya ku Lilongwe komanso Chinkhoma ukuyembekezeka kutsekedwa pa 8 October chaka chino ndipo wa Mzuzu udzatsekedwa pa 24 mwezi omwewu wa October.

Wolemba: Mercy Kaliati

 A polisi mu mzinda wa Lilongwe amanga  mnyamata wa zaka 18 Aubrey Chidothi ati pomuganizira amawabera  lamya  za m'manj...
01/10/2025



A polisi mu mzinda wa Lilongwe amanga mnyamata wa zaka 18 Aubrey Chidothi ati pomuganizira amawabera lamya za m'manja anthu oyendetsa Kabanza komanso ena omwe amapita ku polisiyi kukazonda abale awo omwe anamangidwa.

Malinga ndi m'neneli wa polisi ya Lilongwe, a Hastings Chigalu, Chidothi amatha kupezaka a Kabaza ndikupita nawo ku polisi ya Lilongwe-yi ndikuwauza kuti awabwereke foni yawo ndipo awadikire pa khomo lolowera pamene akukathamangitsa malonda ena mkati mwa polisiyi koma akatero amakhala kuti akatulukira njira ina osabweraso.

A Chigalu atiso Chidothi amatha kuwapeza anthu omwe akukazonda abale awo omwe anamangidwa pa polisiyi ndikuwauza zoti awapatse ma foni awo awathamangatsire limande ya abale awo koma akamupatsa amapezeka kuti wasowa mu mpandawu osaonekaso.

Chidothi anamumangaso kumayambiliro kwa chaka chino ndi mulandu ngati omwewu pamene nthawiyo anaba ma foni atatu ndipo adagamulidwa ndi bwalo la milandu kuti akakhale ku ndende kwa miyezi 8.

Wolemba : Eliot Tandani

 Mtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera akakhala nawo pa mwambo wolumbilitsa yemwe wasankhidwa kumene kukhala mtso...
01/10/2025



Mtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera akakhala nawo pa mwambo wolumbilitsa yemwe wasankhidwa kumene kukhala mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika ndi wachiwiri wake Dr.Jane Mayemu Ansah.

Mwambowu uchitika loweluka pa 4 October pa bwalo la zamasewero la Kamuzu mu m'zinda wa Blantyre kuyambira nthawi ya 8 m'mawa.

Poyankhula ndi Nkhoma Synod Radio mlembi wamkulu mu unduna wa zofalitsa nkhani Baldwin Samuel Chiyamwaka watsimikiza za nkhaniyi ponena kuti komiti yomwe ikuyendetsa mwambowu yadziwitsidwa kuti Dr. Chakwera adzakhala nawo pa mwambowu.

Iwo atinso kupatula Dr.Chakwera, atsogoleri akale ena a dziko lino komanso mabungwe a m'maiko ena akakhala nawonso pa mwambowu.

01/10/2025

 Gawo lomaliza lampikisano wamasewero ampira wamanja wa Nico top 12 netball cup likuyembekezeka kuchitika kuyambila lach...
01/10/2025



Gawo lomaliza lampikisano wamasewero ampira wamanja wa Nico top 12 netball cup likuyembekezeka kuchitika kuyambila lachisanu pa 03 October mpaka lamulungu 05 October 2025 pabwalo la Don Bosco mumzinda wa Lilongwe.

Mpikisanowu, ukubweletsa pamodzi matimu omwe anachita bwino muzigawo zinai zamdziko muno ndipo chigawo chilichose chikhale chikuimilidwa ndimatimu atatu.

Ndipo mndandanda wamatimu omwe akhale akulimbilana ukatswiri uli motere.

NORTH
-Ekwendeni Resource
-Moyale Sisters
-Mzimba queens

CENTRAL
-Blue Eagles
-Civonets
-Young Eagles

SOUTH
-Kukoma Diamonds
-Tigresses
-Blantyre Tremors

EAST
-Genius
-Prison Queens
-Airforce Falcons

Wolemba Madalitso Sainani

 TCHAMANI WAMA RED CARD SANATAYE CHIPANGANO NGAKHALE WAPAMBANATimu ya Chelsea yomwe ikudziwika ndikuchita kusaweluzika,y...
01/10/2025



TCHAMANI WAMA RED CARD SANATAYE CHIPANGANO NGAKHALE WAPAMBANA

Timu ya Chelsea yomwe ikudziwika ndikuchita kusaweluzika,yagonjetsa Benfica 1-0 usiku wadzulo mumasewero amu UEFA Champions League.

Chelsea inapeza chigoli chake pamphindi 18 zachigawo choyamba pamene mpira omwe anamenya Alejandro Garnacho, unakumanizana ndiphazi laosewera wa Benfica Richard Rios amene anazigoletsera yekha.

Ngakhale zimaoneka kuti Chelsea ikhoza kumaliza masewero adzulo ili ndiosewera okwana, zinthu zinachitika mwachizilowezi pamphindi 90+6 pamene Joao Pedro analandila khadi lachikasu lachiwiri zomwe zinapangitsa awonetsedwe khadi lofiira lomwe linamulora kukapuma mwachangu.

Izi zikutanthauza kuti kuti tsopano mumasewero atatu otsatana, Chelsea yakhala ikulandila ma Red Card zomwe ambiri afika pozolowera.

Wolemba Madalitso Sainani

 LIVERPOOL IKHOZA KUTHERA MMANJA MWAMATIMU PAMENE YAFASO DZULOTimu ya Liverpool ikupitilira kudutsa munyengo zowawa pame...
01/10/2025



LIVERPOOL IKHOZA KUTHERA MMANJA MWAMATIMU PAMENE YAFASO DZULO

Timu ya Liverpool ikupitilira kudutsa munyengo zowawa pamene yagonjaso 1-0 nditimu ya Galatasaray mumasewero amumpikisano wa UEFA Champions League omwe aseweredwa usiku walachiwiri mdziko la Turkey.

Chigoli cha Galatasaray chinabwera pamphindi 16 zachigawo choyamba kudzera papenate yomwe anagoletsa ndi victor Osimhen.

Kumathero kwasabata yapitayi, Liverpool inagonjaso 2-1 nditimu ya Crystal Palace mumasewero amuligi ya EPL zomwe zikupeleka chiopsezo kuti timuyi ikhoza kuthera mmanja mwamatimu.

Olemba Madalitso Sainani

Address

Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nkhoma Synod Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nkhoma Synod Radio:

Share