Nkhoma Synod Radio

Nkhoma Synod Radio Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Nkhoma Synod Radio, Broadcasting & media production company, Lilongwe.
(1)

Nkhoma Synod Radio is a christian Radio station under the C.C.A.P Nkhoma Synod, which intends to bring people closer to God using well produced Christian Programs

 Bungwe lowona za zisankho la Civil Society Elections Integrity Forum (CSEIF) lati likhazikitsa ndondomeko yobweretsa po...
25/06/2025



Bungwe lowona za zisankho la Civil Society Elections Integrity Forum (CSEIF) lati likhazikitsa ndondomeko yobweretsa poyera maina a zipani zandale komanso atsogoleri ake omwe akhale akulimbikitsa m'chitidwe wa ziwawa pa ndale panthawi ya misonkhano yokopa anthu pofuna kuti anthuwa adzipatsidwa zilango zokhwima.

Izi zikudza pomwe kwangotsara sabata ziwiri kuti bungwe loyendetsa zisankho la MEC litsegulire nyengo ya misonkhano yokopa anthuyi.

Wapampando wa bungweli Benedicto Kondowe wati kudzera ku ndondomekoyi bungweli lizichita kafukufuku wokhudza nkhanizi ndi kutulutsa malipoti ake.

Katswiri pankhani zandale Dr. George Chaima wati pakadali pano zipani zina zikukhudzidwa ndi m'chitidwe wa ziwawa pa ndale ndipo wati akuyembekezeka kuti ndondomekoyi ithandiza kuchepetsa izi panthawiyi.

Wolemba: Billy Amos

25/06/2025



Mnyamata wa zaka 19 wamwalira pa ngozi yapansewu yomwe yachitika m'bandakucha wa lero ku Neno.

Mneneli wa polisi ya Neno Rabecca Msoliza wati mnyamatayu ndi John Nyirenda wa m'mudzi mwa Matemba kwa mfumu yaikulu Mlauli ku Neno.

Iwo ati mnyamatayu pamodzi ndi anthu ena khumi adakwera truck ina kulowera kwa Chifunga.

Koma atafika pa Magaleta, dalaivala adakanika kuongolera bwino chifukwa cha vuto lina ndipo idagudubuzika.

Kutsatira ngoziyi, mnyamatayu adavulala kwambiri m'mutu ndipo wamwalira akulandira thandizo la mankhwala pa chipatala cha Magaleta.

 Apolisi ku Zalewa m'boma la Neno amanga dalaivala ndi kondakitala wa minibus ina kaamba powaganizira kuti apezeka ndi c...
25/06/2025



Apolisi ku Zalewa m'boma la Neno amanga dalaivala ndi kondakitala wa minibus ina kaamba powaganizira kuti apezeka ndi copper wire yemwe akumuganizira kuti ndi wobedwa.

Mneneli wa polisi ya Neno Rabecca Msoliza wati awiriwa ndi Assan Bwaila wa zaka 54 komanso Goodson Mpotazingwe wa zaka 30.

Iwo ati apolisi adaimitsa minibus yomwe Assan amayendetsa pa roadblock ya Zalewa pomwe amachokera ku Balaka kulowera ku Blantyre.

Iwo adapezeka ndi ma copper wire-yu mu chikwama koma adalephera kuwonetsa kalata zake.

Apa ndi pomwe apolisi adamanga anthuwa ndipo akuyembekezeka kuwonekera ku bwalo la milandu posachedwa.

 Apolisi ku Phalombe amanga nzika zitatu za m'dziko la Mozambique poziganizira kuti zapezeka ndi ma litres 600 a mafuta ...
25/06/2025



Apolisi ku Phalombe amanga nzika zitatu za m'dziko la Mozambique poziganizira kuti zapezeka ndi ma litres 600 a mafuta a galimoto popanda chilorezo.

Mneneli wa polisi ya Phalombe Sergeant Jimmy Kapanja wati makosanawa ndi Frank Chinowa wa zaka 29, Frank Laston 25 ndi Charles Mwaitana 25.

Iwo ati akanganyawa dzulo amafuna kunyengelera wa polisi wina pa border ya Likangala kuti awathandize kutulutsa mafuta-wa pa njinga ya moto kupita nawo ku Mozambique ponena kuti amupatsa ndalama izi zikatheka.

Koma apa apolisi adamanga anthuwa ndikulanda mafuta-wa.

A Kapanja ati atatu-wa akaonekera ku bwalo la milandu posachedwa.

25/06/2025



Unduna woona za chitetezo cha m'dziko waletsa anthu kuvala zovala za makaka olingana ndi unifolomu za nthambi za chitetezo.

Izi ndi malinga ndi uthenga womwe undunawu watulutsa, ndipo wasainidwa ndi nduna mu undunawu, Ezekiel Peter Ching'oma.

Malinga ndi uthenga-wu, aliyense wonyozera izi, adzalandidwa zovala zotero komanso kutengeredwa ku bwalo la milandu.

Undunawu wati chiletsochi chayamba kale kugwira ntchito.

 TCHAMANI NDI ARSENAL, DZINA LASOWABungwe loyendetsa masewero ampira wamiyendo ku ulaya la Union of European Football As...
25/06/2025



TCHAMANI NDI ARSENAL, DZINA LASOWA

Bungwe loyendetsa masewero ampira wamiyendo ku ulaya la Union of European Football Associations(UEFA), latulutsa mndandanda wamatimu khumi amphavu pakadali pano kutengera ndimomwe achitira muzikho ndi maligi osiyanasiyana.

Mndandandawu uli motere

1.Real Madrid 144 Points
2.Manchester City 138 Points
3.Bayern Munich 135 Points
4.Liverpool 126 Points
5.Paris Saint Germain 119 Points
6.Inter Milan 116 Points
7.Chelsea 109 Points
8.Borrusia Dortmund 107 Points
9.AS Roma 105 Points
10.Barcelona 103 Points

Kwa amene tikudabwa kuti timu yathu sikuwonekapo, mwina tidikile patsamba lachiwiri.

25/06/2025



Nkhoma Synod Radio yapeza kuti mitengo yashuga yayamba kutsika mashopu ena mu m'zinda wa Lilongwe.

Posachedwapa mitengo yashuga inafika mpaka MK7,000.00 koma pano mitengoyi m'ma shopu ena yatsika mpaka yafika pa MK3,900.00.

Poyankhula ndi Nkhoma Synod Radio m'neneli waunduna owona za malonda ndi mafakitale Patrick Botha wati ngakhale zinthu zili chonchi komabe mtengo wovomelezeka wogulira shuga ndi MK2950.00 monga momwe sitolo zina zikugulitsira.

Malingana ndi a Botha boma ndilodzipeleka kuwonetsetse kuti shuga akupezeka ngambwingambwi palipose komanso akugulitsidwa pamtengo wovomelezeka m'dziko muno.

Wolemba: Alinafe Jonas

25/06/2025

 CHIMWEMWE CHIDZA MAMAWA, FLAMENGO KOMASO CHELSEA AFIKA MUNDIME INAMatimu a Flamengo ndi Chelsea ndiomwe azigulira malo ...
25/06/2025



CHIMWEMWE CHIDZA MAMAWA, FLAMENGO KOMASO CHELSEA AFIKA MUNDIME INA

Matimu a Flamengo ndi Chelsea ndiomwe azigulira malo mundime yamatimu 16 yampikisano wa FIFA Club World Cup kuchokera mugulu D lampikisanowu.

Izi zili chomwechi potengera ndizotsatira zamasewero amugululi omwe aseweredwa m'bandakucha walero.

Chelsea yagonjetsa Esperance 3-0 ndizigoli za Tosin Adarabioyo, Liam Delap ndi Tyrique George pamphindi 45+3, 45+5 ndi 90+7.

Mumasewero ena matimu a Los Angeles komaso Flamengo alepherana pogoletsana chigoli chimodzi chimodzi.

Flamengo yamaliza pamwamba pagululi ndimapoints 7 ndipo idzakumana ndi Bayern Munich mundime yamatimu 16 pamene Chelsea yomwe yamaliza pachiwiri ndimapoints 6, idzasewera ndi Benfica.

Mukhale ndi mmawa opambana.

 Chigawo choyamba chatha ndipo Chelsea ikukapumulira ikutsogola ndizigoli ziwiri kwachilowele.Zigolizi wagoletsa ndi Tos...
25/06/2025



Chigawo choyamba chatha ndipo Chelsea ikukapumulira ikutsogola ndizigoli ziwiri kwachilowele.

Zigolizi wagoletsa ndi Tosin Adarabioyo komaso Liam Delap pamphindi 45+3 ndi 45+5.Zigoli zonsezi wathandizira ndi Enzo Fernandes.

Mumasewero ena amugulu D, matimu a Los Angeles komaso Flamengo akukapumulira akufunana mphavu.

Chelsea 2-0 Esperance
Los Angeles 0-0 Flamengo

 NGONGOLE ZANU ZAFIKA PAMWANA WAKANA PHALA CHONCHO PITANI KAYE KU LIGUE 2Timu ya Olympic Lyon yatulutsidwa muligi yaikul...
24/06/2025



NGONGOLE ZANU ZAFIKA PAMWANA WAKANA PHALA CHONCHO PITANI KAYE KU LIGUE 2

Timu ya Olympic Lyon yatulutsidwa muligi yaikulu yampira wamiyendo yamdziko la France kaamba kokhala ndingongole zandalama zochuluka.

Malingana ndi DNCG kudzera muchikalata chake, timu ya Lyon yakhala ikuchenjezedwa zakuti ichepetseko ngongolezi, koma mmalo mwake ngongole imangokulirakulira.

Ngongole yonse ikuyandikila €500 million ndipo Lyon ikhale ikusewera mu Ligue 2.

Lyon ili ndimwai okamang'anala zachigamulochi.

Yalembedwa ndi Sky Sports ndipo yatanthauzilidwa ndi Madalitso Sainani

 Apolisi ku Chikwawa amanga anthu awiri powaganizira kuti adaba ndikuwononga ma meter a Southern Region Water Board a nd...
24/06/2025



Apolisi ku Chikwawa amanga anthu awiri powaganizira kuti adaba ndikuwononga ma meter a Southern Region Water Board a ndalama zokwana 1.7 million kwacha.

Wachiwiri kwa mneneli wa polisi ya Chikwawa Constable Chance Mfune wati awiriwa ndi Flyton Ganizani wa zaka 19 ndi Mphatso Seleman wa zaka 18.

Iwo ati apolisi akhala akulandira ma uthenga akubedwa ndi kuononga katundu wa bungwe la Southern Region Water Board.

Atachita kafukufuku akwanitsa kumanga akanganyawa ndipo iwo apezeka ndi ma meter okwana 8.

A Mfune ati awiriwa akaonekera ku bwalo la milandu posachedwa komwe akayankhe mlanduwu.

Address

Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nkhoma Synod Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nkhoma Synod Radio:

Share