![Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo ikupitilira kudziwitsa mtundu wa a Malawi kuti Namondwe DIKELEDI akadal...](https://img4.medioq.com/989/443/595559529894439.jpg)
14/01/2025
Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo ikupitilira kudziwitsa mtundu wa a Malawi kuti Namondwe DIKELEDI akadali m’nyanja ya m’chere ya pakati pa maiko a Madagascar ndi Mozambique.
Malingana ndi Nthambi ya Zanyengoyi, Namondweyu ali kufupi ndi mzinda wa Angoche kuchigawo cha Nampula pa mtunda wapafupifupi makilomita 460 kuchokera ku
Malawi.
Komabe, Namondweyu wachepako mphamvu pang’ono ndipo tsopano akupitiriza kuyenda ndi liwiro la makilomita 13 pa ola kumalowera kum’mwera chakuzambwe kwa nyanja ya mchere ya pakati pa Madagascar ndi Mozambique.
Namondwe Dikeledi, akuyembekezeka kukula mphamvu pofika Lachitatu.
Kuthekera kwakuti Namondweyu angafike ku Malawi kuno ndi kochepa kwambiri, komabe kuyambira leropa 14 January 2025 namondweyu akuyembekezeka kulimbikitsa mvula m’madera ena a ku Malawi, yomwe ikuyembekezeka kudzagwa yamphamvu m’madera ena.
Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo yati ipitilira kupereka kauniuni wa momwe namondweyu akuyendera.
Chidziwitsochi chidzawunikidwanso Lachitatu pa 15 January, 2025.