Nyungwe FM

Nyungwe FM Nyungwe FM 107.6MHz is located near Thabwa Road Block in Chikwawa district. Voice of the valley.

 Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo ikupitilira kudziwitsa mtundu wa a Malawi kuti Namondwe DIKELEDI akadal...
14/01/2025



Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo ikupitilira kudziwitsa mtundu wa a Malawi kuti Namondwe DIKELEDI akadali m’nyanja ya m’chere ya pakati pa maiko a Madagascar ndi Mozambique.

Malingana ndi Nthambi ya Zanyengoyi, Namondweyu ali kufupi ndi mzinda wa Angoche kuchigawo cha Nampula pa mtunda wapafupifupi makilomita 460 kuchokera ku
Malawi.

Komabe, Namondweyu wachepako mphamvu pang’ono ndipo tsopano akupitiriza kuyenda ndi liwiro la makilomita 13 pa ola kumalowera kum’mwera chakuzambwe kwa nyanja ya mchere ya pakati pa Madagascar ndi Mozambique.

Namondwe Dikeledi, akuyembekezeka kukula mphamvu pofika Lachitatu.

Kuthekera kwakuti Namondweyu angafike ku Malawi kuno ndi kochepa kwambiri, komabe kuyambira leropa 14 January 2025 namondweyu akuyembekezeka kulimbikitsa mvula m’madera ena a ku Malawi, yomwe ikuyembekezeka kudzagwa yamphamvu m’madera ena.

Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo yati ipitilira kupereka kauniuni wa momwe namondweyu akuyendera.

Chidziwitsochi chidzawunikidwanso Lachitatu pa 15 January, 2025.

 Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera watumiza wachiwiri wake, Dr Michael Usi ku dziko la Mozambique kukayimira ...
14/01/2025



Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera watumiza wachiwiri wake, Dr Michael Usi ku dziko la Mozambique kukayimira dziko lino pa mwambo wolumbiritsa mtsogoleri wa dzikolo, Daniel Tchapo.

Mtsogoleri wakale wa dzikolo, Dr Filipe Nyusi ndi amene wayitana Dr Chakwera pamwambo omwe uchitikire ku Maputo pa 15 January, 2025.

Dr Michael Usi anyamuka m'mawa wa lero pa bwalo la Kamuzu ku Lilongwe ndipo adzabwerera kuno kumudzi Lachinayi pa 16 January, 2025 kudzera pa bwalo la ndege la Chileka mu mzinda wa Blantyre.

Wolemba: Francis Mwale

TAMVANI IZI!Nyungwe NewsroomNyungwe FMAnthu ena akusokoneza pakati pa Joyce Chitsulo MP wa Mwanza West ndi Joy Chitsulo ...
13/01/2025

TAMVANI IZI!
Nyungwe Newsroom
Nyungwe FM

Anthu ena akusokoneza pakati pa Joyce Chitsulo MP wa Mwanza West ndi Joy Chitsulo aspirant MP wa Chikwawa Central.
M'chiithunzimu muli Joyce Chitsulo MP, kumanzere ndi Joy Chitsulo Shadow MP kumanja.

 Joy Chitsulo wabwera poyera kuwuza anthu okhala m'dera la pakati pa boma la Chikwawa kuti nkhani yofuna kuthetsa njala ...
13/01/2025



Joy Chitsulo wabwera poyera kuwuza anthu okhala m'dera la pakati pa boma la Chikwawa kuti nkhani yofuna kuthetsa njala ndicho chifukwa chachikulu chomwe chamuchititsa kudzayimira ngati Phungu wa Nyumba ya Malamulo m'derali.

Chitsulo wayankhula izi Lamulungu powuza Nyungwe FM yomwe imafuna kudziwa zina mwa ntchito zomwe adzatumikire anthu a m'derali ngati atadzamusankha pa udindowu pa chisankho cha pa 16 September 2025.

Iye wati wasankha kukhala phungu woyima payekha kuti adzatumikire kwathunthu anthu okhala m'derali pa ntchito za ulimi kuti adzathetse njala.

Pothilirapo ndemanga pa zomwe Chitsulo wanena, wapampando wa Komiti yokopa anthu ku chigawo cha Dyeratu, a Patricia Kanyerere ati komitiyi igwira ntchito yomemeza anthu kukalembetsa mayina mu kaundula wapadera wa chisankho akadzatsekulidwa.

Joy Chitsulo anasankha chizindikiro cha tsache pa ulendo wa ku chisankho Chachikulu cha pa 16 September chaka chino.

Wolemba: Francis Mwale

 Yemwe akufuna kudzapikisana nawo pa udindo wa Phungu wa Nyumba ya Malamulo Kumpoto kwa Chikwawa, Wyson Bush wati wayala...
13/01/2025



Yemwe akufuna kudzapikisana nawo pa udindo wa Phungu wa Nyumba ya Malamulo Kumpoto kwa Chikwawa, Wyson Bush wati wayala zitukuko zogwirika zomwe akufuna kudzakwaniritsa akadzatenga udindowu pa 16 September 2025.

Bush, yemwenso ndi khansala wa m'dera la Mwamphanzi mu chipani cha DPP m'derali wati adzapambana ndi mavoti ochuluka chifukwa ndiyekhayo yemwe ali ndi kuthekera kutukula derali.

"Anthu okhala Kumpoto kwa Chikwawa adzapeza mwayi wa ngongole za NEEF, maphunziro apamwamba, umoyo wathanzi ndi zitukuko zina zofunikira ku derali pogwiritsa bwino ntchito ndalama za m'thumba la CDF." anatero Bush.

Wyson Bush anakhalapo wapampando wa Khonsolo ya Chikwawa kuyambira mwezi wa August 2023 mpaka August 2024 ndipo wati cholinga chake ndi kutukula miyoyo ya achinyamata ndi amayi pa chuma.

 Bungwe la Southern Region Cane Growers Association (SRCGA) latsimikizira alimi a mzimbe a Phata kuti utsogoleri wabwino...
13/01/2025



Bungwe la Southern Region Cane Growers Association (SRCGA) latsimikizira alimi a mzimbe a Phata kuti utsogoleri wabwino ndi wamasomphenya ndi umene ungatukule magulu a alimi a mzimbe.

Mlembi Wamkulu wa bungwe la Sugarcane Growers Association of Malawi (SUGAM), a Alex Mtengula ayankhula izi Lolemba potsekukira maphunziro a masiku atatu osula adindo otsogolera magulu a alimi a Phata omwe akuchitikira ku Hope Lodge ku Dyeratu m'boma la Chikwawa.

A Mtengula anati; "Kulumikizana kwabwino pakati pa atsogoleri, alimi ndi makampani ogula mzimbe kungapititse patsogolo chitukuko cha ulimi wa mzimbe."

M'mawu ake, Mlembi Wamkulu wa Phata Cane Growers Association, a Esimy Tinka Chitsulo ati kudzera mu maphunziro omwe akulandira, awachotsa mantha ndipo atsimikiza zotumikira alimi anzawo moyenera.

Southern Region Cane Growers Association (SRCGA) ili ndi magulu awiri a alimi a Phata komanso Kasinthula pansi pa bungwe lalikulu la Sugarcane Growers Association of Malawi (SUGAM) momwe muli magulu 19 a alimi a mzimbe.

Wolemba: Francis Mwale

 Mtsogoleri wa alimi a mzimbe ku Malawi m'bungwe la Sugarcane Growers Association of Malawi (SUGAM) wadzudzula boma kamb...
13/01/2025



Mtsogoleri wa alimi a mzimbe ku Malawi m'bungwe la Sugarcane Growers Association of Malawi (SUGAM) wadzudzula boma kamba kochedwetsa kuvomereza lamulo la shuga.

A Robert Dziweni ayankhula izi Lolemba pa 13 January 2025 pomwe Nyungwe FM imafuna kudziwa za momwe bungwe lawo likuchita popititsa patsogolo ulimi wa mzimbe m'dziko muno.

Pamenepa, a Dziweni apempha boma kuti lifulumizitse dongosolo lotengera lamuloli ku Nyumba ya Malamulo kuti aphungu alivomereze ndi kuyamba kugwira ntchito.

"Kunyalanyaza kwa boma kuvomereza lamulo la shuga zikusonyeza kuti silikuyikirapo mtima pa ulimiwu. Boma lomweli lavomereza ma bilu a mbewu zina, ndiye kulephera kovomera za lamulo ili kukutipatsa mafunso ochuluka," anatero a Dziweni.

Powonjezerapo, Iwo ati alimi a mzimbe akuvutika kupeza phindu kamba koti makampani ogaya mzimbe amapsinja alimiwa ndi njira zomwe amatsata ponyamula ndi kugula mzimbe zawo.

Malingana ndi mtsogoleri wa bungwe la SUGAM-yu, bungweli lapereka malire a chaka chino kuti boma likhale litayankha za pempho lawo.

Tinayetsetsa kuti tiyankhulane ndi aku boma komanso mbali zina zokhudzana ndi zamalimidwe koma anati tiwapatse mpata okwanira asanayankhe.

Wolemba: Francis Mwale

13/01/2025



Wapampando wa Komiti ya Chikho cha masewero a mpira cha Joy Chitsulo ku zone ya Dyeratu, Patricia Kanyerere wati apitilira kulimbikitsa masewero pakukhazikitsa zina za masewero osiyanasiyana.

Kanyerere anayankhula izi Lamulungu pa 12 January popereka chikho ndi mendulo kwa matimu atatu omwe anachita bwino mu chikho cha Joy Chitsulo omwe anaseweredwa Loweruka ndi Lamulungu pa bwalo la Mitole ku Dyeratu.

Timu ya Dyeratu Fisheries ndi akatswiri a chikho cha Joy Chitsulo Shadow MP woyima payekha ku dera la pakati pa Chikwawa.

Fisheries yatenga chikho cha ndi mendulo za golide, mpira ndi K60, 000 itagonjetsa Namalindi FC ndi zigoli 3 kwa 1.

Mphunzitsi wa Dyeratu Fisheries Gadiola Widze anati Timu yake inakonzekera bwino kuti ikhale akatswiri.

M'mawu a mphunzitsi wa Namalindi FC Clarick Malasha anati Timu yake yagonja kamba koti anyamata ake anali otopa ndi masewero akathithi omwe anasewera.

Mu Bonanza-yi munalowa matimu anayi a Dyeratu Fisheries, Namalindi FC, Chinangwa Blues ndi Power Dynamos.

13/01/2025



Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo m'dziko muno yati a Malawi adziwe kuti Namondwe DIKELEDI
akadali m’nyanja ya m’chere ya pakati pa maiko a Madagascar ndi Mozambique pa mtunda makilomita wapafupifupi 500 kuchokera ku Malawi.

Iyo yati Namondweyu akuyenda ndi liwiro la makilomita 17 pa ola kumalowera kum’mwera chakuzambwe kwa nyanjayi molunjika ku gombe la Mozambique ku Nampula.

Kuthekera kwakuti Namondweyu angafike ku Malawi kuno ndi kochepa kwambiri, komabe kuyambira
Lachiwiri pa 14 January 2025 namondweyu adzalimbikitsa mvula m’madera ena ku Malawi, kuyambira
kumpoto mkumafalikira m’madera ambiri yomwe ikuyembekezeka kudzagwa yamphamvu m’madera ena.

Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo yati ipitilira kupereka kauniuni wa momwe
namondweyu akuyendera.

Akatswiri a zanyengowa akuyembekezereka kudzaperekanso chidziwitsochi chikadzawunikidwanso Lachiwiri pa 14 January 2025.

11/01/2025



Kunali chipwirikiti ku Nkhate masana Loweruka pa 11 January 2025, pomwe anthu a madera a mfumu yaikulu Mphuka ku Thyolo amalandira chimanga cha m'ndondomeko ya katambalale.

Malingana ndi mai omwe anali pasukulu ya Nkhate pomwe pamachitikira dongosololi, omwe ati tisawatchule dzina, awuza Nyungwe FM kuti chipwirikitichi chinayamba kamba koti oyendetsa dongosolo la kagawidwe ka chimanga omwe ndi makomiti a ADC, VDC ndi mafumu amapereka mpata kwa anthu omwe akuti amagula chimanga chaulerechi.

Mayiwa ati m'modzi mwa abambo oganiziridwa omwe amayenda ndi amfumu a Chikunkhu ati bamboyu waleletsedwa kangapo anthu okwiya atamugwira kuti amumenye.

Mayiwa atinso anthu omwe sanalandire chimangachi ambiri akuoneka ochokera kwa mfumu Chikunkhu zomwe ati zinawadabwitsa kwambiri.

Nyungwe FM itayamba kutsatira ndi kufufuza nkhaniyi mwachidwi, bwanankubwa wa Boma la Thyolo a Hudson Kuphanga ati vutoli likuoneka kuti gwero lake ndi mafumu ndi akomiti ya kumudzi yomwe anaisankha kuti igwire ntchitoyi.

Iwo aloza chala mafumu a kwa mfumu yaikulu Mphuka pandondomeko zomwe anatsata pogawa chimangachi.

Masiku atatu adutsawo , anthu amidzi yakumeneku monga Chikunkhu, Mpino, Mphera, Mathotho , ndi ena opindula ndi ndondomekoyi anafunsidwa kupereka ndalama yoti alipile alonda omwe amayang'anira chimangachi ndipo ndalama yomwe anatolera ndi K250,000.

Wolemba: Jaison Chiyembekezo

Zampira!Bonanza ya Joy Chitsulo K800,000 Trophy iliko masana ano pa bwalo la Mitole ku Dyeratu.1:00pm; Chinangwa Blues v...
11/01/2025

Zampira!
Bonanza ya Joy Chitsulo K800,000 Trophy iliko masana ano pa bwalo la Mitole ku Dyeratu.

1:00pm; Chinangwa Blues vs Namalindi FC.

3:30pm; Dyeratu Fisheries vs Power Dynamos FC.

 Nthambi ya za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo yati lero Loweruka Namondwe DIKELEDI akupitilira kukula mphanvu ndipo tsop...
11/01/2025



Nthambi ya za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengo yati lero Loweruka Namondwe DIKELEDI akupitilira kukula mphanvu ndipo tsopano ali paliwilo la makilomita 22 pa ola.

Namondweyu ali pa
mtunda wapafupifupi makilomita 1680 kuchokera ku Malawi.

Akatswiri a Zanyengowa ati kauniuni wa namondweyu akupitilira kusonyeza kuti afika m’nyanja ya m’chere ya pakati pa maiko a Madagascar ndi Mozambique atadutsa ku mpoto kwa Madagascar lero pa 11January 2025.

Pakali pano Namondweyu sakuonetsa chiopsyezo chilichonse ku dziko lino la Malawi m’masiku awiri akudzawa.

Powonjezerapo, Iwo ati pali mwayi wa mvula yomwe ingalimbikitsidwe ndi DIKELEDI kuyambira Lachiwiri pa 14 January 2025pamene adzisuntha kutalikirana ndi dziko la Malawi.

Nthambi Yoona za Nyengo ndi Kusintha kwa Nyengoyi yati ipitilira kupereka kauniuni wa momwe namondweyu akuyendera, kotero idzatulutsanso chidziwitso chounikiranso za namondweyu Lamulungu pa 12 January, 2025.

 Ku Chikwawa, apolisi akuti atsekera m'chitokosi chawo mayi Zione Makungwa atawapeza ndi mapaipi anthilira okwana khumi ...
11/01/2025



Ku Chikwawa, apolisi akuti atsekera m'chitokosi chawo mayi Zione Makungwa atawapeza ndi mapaipi anthilira okwana khumi a kampani ya Illovo

Wofalitsa nkhani za apolisi m'bomali, a Dickson Matemba ati mayi Makungwa adamangidwa Lachisanu pa 10 January 2025 akufuna kudutsa pa malo achipikisheni a Thabwa pa galimoto yomwe nambala yake ndi BU1766.

Malingana ndi zomwe akuluakulu a kampani ya Illovo anena, katunduyu adabedwa pakati pa 8 ndi 9 January 2025 ndipo ndi wa ndalama zokwana K1,323,000.

Mayi Zione Makungwa womwe amachokera m'mudzi mwa Sekeni ku Nchalo kwa mfumu yaikulu Lundu, akhale akuyankha mlandu womwe awatsekulira posachedwa ku bwalo la milandu.

Wolemba: Francis Mwale

10/01/2025



NYAKWAWA YADZIPHA

Bambo Jamester Sokili, a zaka 80 omwenso anali Nyakwawa Sokili afa atadzimangilira kudenga la kicheni lawo kwa Ngabu.

Malingana ndi wofalitsa nkhani za apolisi m'boma la Chikwawa a Dickson Matemba, Nyakwawayi inadzimangilira Lachinayi pa 9 January, 2025 zomwe azachipatala anatsimikiza kuti yafa kamba kobanika.

Pamenepa, apolisi alangiza anthu kuti apewe mchitidwe wodzipha akakumana ndi mavuto poti kutero sikuthana ndi mavutowo.

Malemuwa amachokera m'mudzi mwa Sokili kwa Mfumu Yaikulu Ngabu m'boma la Chikwawa.

Ndipo padakali pano, sichinadziwike chifukwa chomwe mfumuyi yadziphera.

Wolemba: Francis Mwale

10/01/2025



Bwalo la milandu ku Chikwawa dzulo lagamula a Lucius Danger a zaka 28, a m'mudzi wa Jakobo Mfumu Yaikulu Kasisi m'bomali kuti akagwire ndende kwa zaka zinayi kamba kothyola nyumba ndi kuba katundu wa ndalama zoposa K800,000.

Wofalitsa nkhani za ku polisi m'boma la Chikwawa Dickson Matemba wati mkuluyu adapalamula mlanduwu mu usiku wa pa 12 December chaka chatha.

 Malawi Police Service (MPS) yatsamutsa akuluakulu apolisi oyang'anira m'zigawo kuyambira lero.Izi zadziwika malingana n...
07/01/2025



Malawi Police Service (MPS) yatsamutsa akuluakulu apolisi oyang'anira m'zigawo kuyambira lero.

Izi zadziwika malingana ndi kalata yomwe taona yomwe ikusonyeza kuti Komishonala Chikondi Chingadza awasamutsa ku Chigawo Chakumwera Kumvuma ndipo awatumiza ku Chigawo Chakumvuma.

Komishonala Dr. Noel Kayira atumizidwa ku Chigawo Chakumwera Kumvuma kuchoka ku Chigawo Chakumwera Kuzambwe cha apolisi ndipo pamalo pawo palowa Komishonala Emmanuel Soko.

Yemwe anali mkulu wa chigawo chakumvuma, Komishonala Babra Tsiga aziyang'anira chigawo chapakati chakumwera cha apolisi.

Mneneri wa apolisi m'dziko muno, a Peter Kalaya sadayankhepo kathu kamba kotanganidwa ndi ntchito zina.

Wolemba: Francis Mwale

 Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera wasankha mkulu wa Banki ya Reserve watsopano, Dr Macdonald Mafuta Mwale.M...
06/01/2025



Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera wasankha mkulu wa Banki ya Reserve watsopano, Dr Macdonald Mafuta Mwale.

Mlembi ku ofesi ya mtsogoleri wa dziko ndi nduna, a Colleen Zamba alengeza za kusankhidwa kwa Dr Mwale kudzera mu kalata yomwe alemba lero pa 6 January, 2025.

"Komiti yoona zolemba anthu ntchito m'maudindo akuluakulu m'boma ya Public Appointments Committee (PAC) ikuyembekezereka kutsimikiza Dr Macdonald Mafuta Mwale pa udindowu." yatero mbali imodzi ya kalatayi.

Mtsogoleri wa dziko linoyu wasankhanso Dr Kisu Simwaka pa udindo wa wachiwiri kwa mkulu wa Banki ya Reserve.

Dr Macdonald Mafuta Mwale asankhidwa pa udindowu kulowa pa malo pa Dr Wilson Banda omwe adali mkulu wa Banki-yi.

Wolemba: Francis Mwale

06/01/2025



Pamene mvula yobzalira yayamba kugwa m’madera ambiri, alimi ena m’boma la Chikwawa ati sakudziwa komwe angapeze mbewu ya chimanga yoti abzale m’minda yawo.

Ena mwa alimi okhala m’dera la mfumu yaikulu Kasisi akubzala chimanga chachikasu chomwe adalandira mu ndondomeko ya katambalale chomwe boma likupereka kwa anthu omwe adakhudzidwa ndi Namondwe Freddy komanso ng’amba.

Mkulu wa Mgwirizano CBO a William John ati ambiri mwa alimiwa adalephera kugula mbewu kudzera mu ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo yomwe boma lidakhazikitsa ati kamba ka umphawi ndi mliri wa njala omwe ulipo m’dera lawo.

Anthuwa, omwe akuoneka kuti asimidwa akuti anabzala mbewu chimanga chomwe adalandira mu ndondomeko ya Boma ya katambalale poganiza kuti chitha kumera.

"Alimi ambiri sadakwanitse kugula mbewu pa mtengo wa K25,000 mu ndondomeko ya zipangizo zaulimi zotsika mtengo za AIP," adatero a John.

Mayi Zyolin Nsina a kwa Kasisi ati ng'amba idawononga mbewu yomwe adabzala ndipo yotsalayo adadya pofuna kudzipulumutsa ku mliri wa njala.

Tinabzala chimanga cholandirachi koma sichidamere, sichidamere changofera m'mapando ndiye tikupempha boma ndi mabungwe akufuna kwabwino kuti atithandize ndi mbewu." Adatero mayi Nsina.

Padakali pano, mlangizi woona za mbewu ku Khonsolo ya Chikwawa, a Francis Masitala alangiza alimiwa kuti azibzala mbewu yopangidwa mwamakono yomwe ndiyopilira ku mavuto odza kamba ka kusintha kwa nyengo yomwe imapereka zokolola zochuluka.

Iwo ati alimi akuyenera kuzindikira kuti sichimanga chonse chomwe chili mbewu.

Wolemba: Francis Mwale

Address

Thabwa Opposite Total Filling Station
Chikwawa

Telephone

+265999704638

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nyungwe FM posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nyungwe FM:

Videos

Share

Category