Nyasaland News

Nyasaland News Follow us for well confirmed news, A true non biased Malawian paper,The news that you can trust. htt

09/05/2026

Munthu agwire ntchito kwa munthu kapena ku kampani akuti akutilanda zintchito, munthu apange business pa yekha akuti achoke azipita dziko la kwao .

Anthu opanda pabwino awa...

09/05/2026

Mmodzi mwa anthu opulumuka pangozi ya Munorurama yochokera kumalawi kuno kupita mdziko La South Africa.

Munthu yu ndi waku Kenya a kufotokoza mmene zinalili.

09/05/2026

Zovuta izi...

Koma chibwanachi tatiyeni tisamachite ndi moyo, moyowu ndi kamodzi, ukapita wapita.
09/05/2026

Koma chibwanachi tatiyeni tisamachite ndi moyo, moyowu ndi kamodzi, ukapita wapita.

KWAVUTA UKU AZUNGU ALIBE MASEWERA:NANGA ABALE MINDA YOLANDA LANDA AKAKAMIZIKA KUIBWEZANSO? Dziko la Zimbabwe lati libwez...
09/05/2026

KWAVUTA UKU AZUNGU ALIBE MASEWERA:

NANGA ABALE MINDA YOLANDA LANDA AKAKAMIZIKA KUIBWEZANSO?

Dziko la Zimbabwe lati libweza minda ikuluikulu kwa alimi 67 achizungu omwe analandidwa mindayi ndi boma la dzikolo.

Alimiwa ndi ena mwa alimi pafupifupi 4000 achizungu omwe analandidwa minda ndi boma la Zimbabwe pansi pa ulamuliro wa mtsogoleri wakale wadzikolo Robert Mugabe kuyambira m'chaka cha 2000.

Nduna yoona zaulimi m'dziko la Zimbabwe Anxious Masuka, wati kubweza kwa mindayi kukutsatira mgwirizano wandalama komanso malonda omwe dziko la Zimbabwe lagwirizana ndimaiko a Germany, Netherlands, Switzerland komanso Denmark.

Malingana ndi nyumba yofalitsa nkhani ya DW Africa, dziko la Zimbabwe likuika ndondomeko zomwe zitathandize kukonzaso ubale wake ndimaiko aku ulaya.

Ubale wadziko la Zimbabwe ndi maiko aku ulaya unasokonekera kutsatira ganizo la Mugabe lolanda azungu minda, zomwe anthu ena amati zinasokoneza chuma cha dzikolo.

09/05/2026

Zulo lachisanu agwira kwambiri ku Port Shepstone,kummwera kwa Dera la KwaZulu-Natal mdziko la South Africa.

Kunali operation ya apolisi ndi a Home Affairs, Nkoyeni local municipality ndi a department of Labour.

Moti anthu 50 amaiko ena agwidwako.

09/05/2026

Zaka wa passover wasokoneza Live ya Habakuk uku..

09/05/2026

Basitu eti akuti onse Peter Sambo ndi Bushiri onse ndi zisiru.

Iyi yokha iyi anyamulanako uku.

Akuti watayidwa ndi amalume ake a dimba chifukwa cha matenda omwe akudwala, pano akugona pansi pa bridge ya kaphuka m'bo...
09/05/2026

Akuti watayidwa ndi amalume ake a dimba chifukwa cha matenda omwe akudwala, pano akugona pansi pa bridge ya kaphuka m'boma la Blantyre.

Purezidenti wa dziko la South Africa, Cyril Ramaphosa, akupemphedwa kuti atule pansi udindo kuchokera kwa mtsogoleri wa ...
08/05/2026

Purezidenti wa dziko la South Africa, Cyril Ramaphosa, akupemphedwa kuti atule pansi udindo kuchokera kwa mtsogoleri wa chipani chotsutsa, Julius Malema, pambuyo poti Khoti Loona za Malamulo (Constitutional Court) lalamula kuti nyumba ya malamulo (parliament) inaphwanya malamulo a dzikolo poletsa njira yomuchotsa pa udindo (impeachment) mu chaka cha 2022.

Malinga ndi BBC, mu 2022 gulu lina lodziyimira pawokha linanena kuti Purezidenti Ramaphosa ayenera kuyankha pa mlandu wokhudza kuba kwa ndalama zokwana madola a ku America $580,000 (pafupifupi MK1.005 biliyoni) zomwe zinali zobisidwa mu sofa kunyumba kwake yakumudzi. Panalinso zodandaula kuti sanalongosole komwe ndalama zimenezo zinachokera.

Komabe, Ramaphosa anakana kuti analakwitsa chilichonse, ndipo njira yomuchotsa pa udindo inalepherekedwa zaka zinayi zapitazo kudzera mu voti ya nyumba ya malamulo.
Tsopano Khoti Loona za Malamulo lalamula kuti kuletsa njirayi kunali kosagwirizana ndi malamulo a dzikolo.

Pambuyo pa chigamulochi, Malema analimbikitsa Ramaphosa kuti atule pansi udindo wake ndi kuyika maganizo ake onse pa mlandu womuchotsa pa udindo.

WAZIPHA POZIMANGIRIRA POTHAWA KUGWIDWA PA MLANDU OKUPHA MKAZI WAKEMnyamatayu Atanva kuti anthu akumusakasaka limodzi ndi...
08/05/2026

WAZIPHA POZIMANGIRIRA POTHAWA KUGWIDWA PA MLANDU OKUPHA MKAZI WAKE

Mnyamatayu Atanva kuti anthu akumusakasaka limodzi ndi apolisi kamba Kakupha mkazi wake ku mzimba, kwapezeka kuti nayenso wadzipha pozimangira kufupi ndi komwe adaphera mkazi wake Keliness masiku atatu apitawa ku Elunyeni.

Address

Opposite Chayamba Building, Along Victoria Avenue Street.
Blantyre
817.9

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nyasaland News posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nyasaland News:

Share