Mibawa TV

Mibawa TV Malawi's Entertainment Channel.
(397)

19/02/2025

Dzuwa Lawala

18/02/2025

Kodi mbali ya kwanuko bizinesi ikuyenda bwanji?

Tamvani mmene Mai Hausi akusimbira lokoma - mpaka kuyamba kugulitsa zitenje pa mtengo wa chipiku!

Nzotheka ndithu! Inunso m***a kukuza Mpamba wa bizinesi yanu.

Tiyimbileni lamya lero pa 312 (mwaulele kwa a TNM okha), kapena 0992 950 051 kuti mukacheze ndi alangizi athu.
WhatsApp: 0998 638 221.

https://finca.mw/


!

 ZOKAMBIRANA ZASOKONEKERA KU NYUMBA YA MALAMULOKusamvana kwabuka  ku nyumba ya malamulo kutsatira pempho la  phungu wade...
18/02/2025


ZOKAMBIRANA ZASOKONEKERA KU NYUMBA YA MALAMULO

Kusamvana kwabuka ku nyumba ya malamulo kutsatira pempho la phungu wadera la kum'mawa kwa mzinda wa Blantyre Sameer Suleman kuti mtsogoleri wa dziko lino atule pansi udindo wake komanso zomwe anayankhula m'nyumbayi azichotse mu m'ndandanda wazokambirana za nyumba ya malamulo (Hansald), ati kamba kopereka uthenga kwa aMalawi omwe ati ndi wabodza.

Izi sizinakondweletse aphungu ambali ya boma omwe motsogozedwa ndi mtsogoleri wa zokambirana m'nyumbayi, Richard Chimwendo Banda amene anati sizowona kuti palibe chomwe a Chakwera apanga pamene a Suleman ndi m'modzi mwa aphungu omwe apindura ndi bomali kuphatikizapo kugwiritsa ntchito ndalama za CDF pafupifupi K240 Million pa chitukuko cha m'dera mwawo.

A Suleman amayankhula m'nyumbayi poyankhapo pa zomwe anayankhula mtsogoleri wa dziko lino lachisanu lapitali zomwe sizinakondweretse aphungu ena ambali ya boma ndipo anayamba kukuwa zomwenso zinadzetsa chisokonezo m'nyumbayi.

Apa chinkulirano komanso phokoso zinakula pamene aphungu ena ambali zonse ziwiri anayamba kuvula majakete awo ndikuyamba kuopsezana zomwe zinachititsa kuti wachiwiri kwa wachiwiri kwa sipikala Aisha Adams ayimitse zokambirana komanso kutulutsa m'nyumbayi phungu wa dera la Salima South, Christopher Joseph Manja atakana kutuluka m'nyumbayi kamba kophwanya mwambo.

Pakadali pano zokambirana zasokonekera ndipo aphungu ambali ya boma alowa mu mkumano wadzidzidzi, nyumbayi isanayambirenso zokambirana.

Olemba: Peter Phiri, Lilongwe

  Bungwe lowona za milingo ya katundu la Malawi Bureau of Standards latsegula Sitolo ya Nu Madina Superette & Butchery m...
18/02/2025


Bungwe lowona za milingo ya katundu la Malawi Bureau of Standards latsegula Sitolo ya Nu Madina Superette & Butchery mu m'zinda wa Mzuzu yomwe bungweli linatseka dzulo kamba kosatsatira malamulo a bungweli.

M'neneri wa bungweli a Wazamazama Katatu ati atayendera sitoloyi dzulo anapeza kuti imagulitsa katundu yemwe nthawi yake yogwilitsira ntchito inatha komanso kosowekera ukhondo kumalo osungirako katundu, ndipo ati zonsezi tsopano zakonzedwa.

A Khan omwe ndi owona ntchito za malonda ku sitoloyi ayamikira bungwe la MBS poyendera sitolo komaso kuwonesetsa kuti akutsatira malamulo, iwo apepesa kwa makasitomala awo ndipo ati kupita chitsogolo awonesetsa kuti akutsatira zonse zofunika.

Wolemba Yankho Kachingwe

 Gulu loyamba la timu yampira wamiyendo wa amayi ya Scorchers lafika m'dziko la Zambia.Timuyi izipita m'magawo ndipo ime...
18/02/2025



Gulu loyamba la timu yampira wamiyendo wa amayi ya Scorchers lafika m'dziko la Zambia.

Timuyi izipita m'magawo ndipo imene yafika lero akuyitsogolera ndi m'modzi mwa aphunzitsi a timuyi Maggie Chombo.

Scorchers ikuyembekezeka kusewera masewero opimana mphamvu kawiri ndi timu ya dziko la Zambia.

Olemba Lucy Kadzongwe, Lusaka, Zambia

 PARLIAMENT ELECTS NEW COMMISSIONER AND PAN-AFRICAN PARLIAMENT REPRESENTATIVEParliament has approved the appointment of ...
18/02/2025


PARLIAMENT ELECTS NEW COMMISSIONER AND PAN-AFRICAN PARLIAMENT REPRESENTATIVE

Parliament has approved the appointment of Mzimba South East MP, Akson Kalayile Banda, as a commissioner for the Parliamentary Service Commission.

Kalayile Banda replaces Noah Chimpeni, who was recently appointed Deputy Minister of Health.

The August House has also replaced newly sworn-in Homeland Minister, Ezikiel Peter Ching’oma, as a representative in the Pan-African Parliament with Dedza Central East MP, Joshua Malango.

According to the Pan-African Parliament’s Rules of Procedure, members holding cabinet positions cannot serve in the assembly.

Written by Peter Phiri, Lilongwe

18/02/2025

Onerani pologalamu ya Zenera la Umoyo lero pa 18 February 2025 nthawi ya 5:30 madzulo pomwe iwunikire za kuphunzitsa ana kusamba m'manja ndi sopo nthawi zonse

18/02/2025

Gawo lolembetsa kuti mutenge nawo mbali mumpikisano wa Battle of Worshippers likupitilirabe.

Mwayiwu usakuphonyeni, lembetsani lero potumiza uthenga wapa WhatsApp ku nambala iyi, 0994266677

18/02/2025


MAKOMITI AMUZIGAWO ATHANDIDZIRE KUPITSA MASEWERO A JUDO PATSOGOLO

Bungwe loyendetsa masewero a judo dziko muno sabata ino lichititsa chisankho chosankha adindo oyendetsa masewerowa mzigawo.

Mlembi wamkulu wa bungwe la Judo Association of Malawi Severia Chalira wati adindo atsopano omwe asakhidwe akukhulupilira kuti athandidzire kupititsa patsogolo masewero a Judo m'dziko muno.

A Chalira ati adindo amzigawo wa athandidzira kuti masewerowa a falikire madera osiyanasiyana a m'dziko muno zomwe zipereke danga kwa anthu ochuluka maka achinyamata omwe ali ndi chidwi chosewera masewerowa kuti luso lawo liwonekere poyera.

Chisankho chi chiyamba lachinayi pa 20 February 2025 ndichigawo chapakati pamene chigawo cha kumpoto ndi kum'mwera chisankho chi adzachita loweruka pa 22 February 2025.

Wolemba David Somba - Mzuzu

 NYUMBA YA MALAMULO YAYAMBA ZOKAMBIRANA NDI APHUNGU 51 OKHAAphungu anyumba ya Malamulo okwana 141 mwa aphungu  193  a md...
18/02/2025


NYUMBA YA MALAMULO YAYAMBA ZOKAMBIRANA NDI APHUNGU 51 OKHA

Aphungu anyumba ya Malamulo okwana 141 mwa aphungu 193 a mdziko muno, ajomba ku zokambirana za aphungu zomwe zili mkati mu mzinda wa Lilongwe .

Mkulu wa Zokambirana m'nyumbayi, Richard Chimwendo Banda ndiye anapepha wachiwiri kwa sipikala Aisha Adams kuti asanayambe zokambiranazi ayambe awerengana kuti alipo angati m'nyumbayi.

Atamaliza kuwerenga aphungu omwe afika mnyumbayi aphungu 51 okha ndiomwe adapezeka m'nyumbayi pa nthawi yomwe zokambirana zimayamba ku nyumba ya Malamulo.

Adams wapepha aphungu kuti azisunga nthawi yoyambira zokambirana.

Olemba Peter Phiri, Lilongwe.

18/02/2025

Sapota Kulimbuli pa Pasaka - Powered By 888bets.

Lero kuyambira 8pm ziliko

Address

Blantyre

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Tuesday 09:00 - 17:00
Wednesday 09:00 - 17:00
Thursday 09:00 - 17:00
Friday 09:00 - 17:00
Saturday 09:00 - 17:00
Sunday 09:00 - 17:00

Telephone

00265999844266

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mibawa TV posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mibawa TV:

Videos

Share