Mibawa TV

Mibawa TV Malawi's Entertainment Channel.
(395)

13/01/2025

Tisanthule Malamulo- Kodi malamulo amati chani ngati munthu akusungidwa kundende chigamulo chisanapelekedwe?

Dont miss Faka Moto today from 4pm, live on Kanema M'manja hosted by DJ Boo.
13/01/2025

Dont miss Faka Moto today from 4pm, live on Kanema M'manja hosted by DJ Boo.

13/01/2025


ANTHU ASAMUKE CHIFUKWA MVULA YAMPHAMVU IKUYEMBEKEZEKA KUGWA

Nthambi yoona za ngozi zogwa mwa dzidzidzi ya DODMA yati anthu akhale tcheru ndikuchoka malo oti ali pachiopsezo chakusefukira kwa madzi ndikupita malo otetezeka.

Izi zili chomwechi pamene nthambi yoona zanyengo yatulutsa malipoti kuti pali kuthekera koti m'dziko muno titha kulandila mvula yamphamvu kuyambira lachiwiri sabata ino.

Malingana ndi m'neneri wa nthambi ya DODMA a Chipiliro Khamula ati anthu omwe akukhala malo oti ali pachiopsezo chakusefukira kwa madzi asazengeleze koma apite akakhale malo otetezeka kuti ateteze miyoyo.

Iwo alangiza makolo omwe ali ndi ana oti akupita m'sukulu zosiyanasiyana kuti awonetsetse ana awo ndiotetezeka m'nyengo imeneyi maka omwe amadutsa m'mitsinje akamapita kusukulu.

Wolemba Salomy Chisi.

 60 ATHLETES EARMARKED FOR TAEKWONDO NATIONAL CHAMPIONSHIP Taekwondo Association of Malawi (TAM) aims to assemble a stro...
13/01/2025


60 ATHLETES EARMARKED FOR TAEKWONDO NATIONAL CHAMPIONSHIP

Taekwondo Association of Malawi (TAM) aims to assemble a strong team of at least 60 athletes for the upcoming national championship, slated for the first half of the year.

The event will serve as a selection platform for the national team, which will represent Malawi in continental and global tournaments.

TAM Vice President Lovemore Masinga revealed the association's plans at the conclusion of the South-Eastern Region Tournament.

The event was part of TAM's efforts to identify top athletes for the national championship, following a similar tournament in the central region as northern region is on the card.

Masinga expressed satisfaction with the athletes' performance across all categories, highlighting the regional tournaments' inclusive nature, which accommodates junior athletes as young as 6 years old.

Madalitso Chidule from Skies Taekwondo Club in Blantyre, who secured a gold medal in female category, praised the tournament for boosting her experience.

"It was my first serious tournament, and it's been great," she said.

Skies Taekwondo Club dominated the competition, collecting 6 gold medals, 3 silver medals, and 2 bronze medals.

They outperformed rival clubs, including Cobbe Barracks, Black Tiger, Blantyre Youth Center, and Lions of Kaning'ina Club.

Blantyre Youth Center Club managed to secure one gold medal.

Picture: Skies Taekwondo Club with trophy.

Reported by Paul Kalaje in Blantyre.

Don't  miss
13/01/2025

Don't miss

 MPUNGWEPUNGWE KU MOZAMBIQUE UTIPATSE PHUNZIRO MU NYENGO YA CHISANKHO CHA MU SEPTEMBERMpungwepungwe omwe ukuchitika m'dz...
13/01/2025


MPUNGWEPUNGWE KU MOZAMBIQUE UTIPATSE PHUNZIRO MU NYENGO YA CHISANKHO CHA MU SEPTEMBER

Mpungwepungwe omwe ukuchitika m'dziko la Mozambique omwe wabadwa kaamba koti anthu kumeneko sakumvana pa zotsatira za chisankho ukuyenera kupereka chenjezo ku dziko la Malawi pa kufunika kochita zokonzekera zake mosamala pofuna kuti chisankho cha mu september chidzakhale chabata ndi mtendere

M'busa Goodson Chitsulo pansi pa mpingo wa Christ Alive Family Church m'boma la Ntcheu ndiye watsindika za kufunika koti adindo m'dziko muno achilimike pa kuphunzitsa anthu za kulolerana komanso mtendere pofuna kupewa kusamvana komwe kumakhalapo pa nthawi yokonzekera zisankho komanso pomwo zotsatira za chisankho zaulutsidwa.

Malingana ndi a Chitsulo boma, mipingo, mabungwe omwe si a boma komanso nthambi zomwe zimakhudzidwa ndi zisankho akuyenera kulimbikitsana kudzera mu mgwirizano pakati pawo pa ntchito yoonetsetsa kuti anthu akuzindikira momwe chisakho chimayendera.

Iwo amayankhula izi m'boma la Dedza pomwe anali mlendo mlendo olemekezeka pa mwambo omwe mpingo wa Christ Alive Family Church m'bomali umakondwelera kuti wakwanitsa zaka makumi awiri, 20, kuyambira pomwe unayamba kutumikira anthu.

Mpingowu unayamba kugwira ntchito zake kuno ku Malawi pa 5 December chaka cha 2004 ndipo uli ndi nthambi zake m'maboma onse a dziko lino.

Wolemba: Horace Tebulo, Dedza

 OTSATIRA CHIPANI ASAMALOWELERE NTCHITO YA APOLISI - AKATSWIRI Kulowelera kagwiridwe ntchito ka nthambi yoona za chitete...
13/01/2025


OTSATIRA CHIPANI ASAMALOWELERE NTCHITO YA APOLISI - AKATSWIRI

Kulowelera kagwiridwe ntchito ka nthambi yoona za chitetezo kuli ndi kuthekera kosokoneza ntchito yolimbana ndi katangale m'dziko muno.

Ena mwa akatswiri olankhulapo pa nkhani zosiyanasiyana mdziko muno a Wonderful Mkhutche komanso a Latim Matenje ndiwo anena izi pomwe anthu ena andale akumalowelera ntchito za nthambizi.

Malinga ndi a Mkhutche, zomwe akumachita anthuwa posonkhana ku polisi munthu wandale akamangidwa ndikuphwanya malamulo kamba koti ndi malo achitetezo.

A Mkhutche ati ngati apolisi atenga munthu pamakhala kuti pali mlandu kotero anthu amayenera kudikirira zotsatira za mlanduwo.

Kuwonjezera apo, katswiri yu wapempha atsogoleri a ndale kuti aziwazindikiritsa otsatira awo za ndondomeko zoyenera kutsata.

Latim Matenje wati apolisi ena amayambitsa dala milandu mwa ndale zomwe zikumaonetsa ngati kuti ena akugwira ntchito pansi pa anthu andale ena.

Matenje wapempha apolisi m'dziko muno kuti azigwira ntchito yawo motsatira malamulo.

"Andale akuyenera kusiya apolisi kuti azigwira ntchito yawo popanda kuwalowerera kulikonse, izi zikapitilira pakhala kukaikirana pakati pa anthu ndi apolisi", watero Matenje.

Sabata yatha, otsatira chipani cha Democratic Progressive - DPP anakasonkhana ku polisi ya Blantyre ndi Lilongwe kutsatira kumangidwa kwa akuluakulu ena a chipanichi a Sameer Suleman komanso a Alfred Gangata.

Wolemba Deborah Kulinji Jenala

Today's  Schedule!
13/01/2025

Today's Schedule!

Don't  miss!
13/01/2025

Don't miss!

 Timu ya Songwe border yati kuchoka pa 20 kufika pa 30 mwezi uno ichititsa ndondomeko yoyesa osewera atsopano ku timuyi....
13/01/2025



Timu ya Songwe border yati kuchoka pa 20 kufika pa 30 mwezi uno ichititsa ndondomeko yoyesa osewera atsopano ku timuyi.

Malingana ndi mmodzi mwa akuluakulu a timuyi a Mike Maulidi ati akuchita izi kuti timu yawo ikhale yolimba mu ligi yayikulu malingana ndikuti abwera kudzakhala.

Kupatulako kuyesa mwayi wa osewera, Sogwe Border yati ikuyembekezereka kuchita mayeso opeza mphunzitsi wa timuyi mawa lino kuti mphunzitsiyu akhale atayamba kugwira ntchito pasanafike pa 20.

Timu ya Songwe Border United imene yalowa kumene mu ligi yayikulu kuchokera m'chigawo chaku mpoto.

Olemba Blessingz Mtika

Kiddies Movie Night: A Magical Adventure Awaits!Gather your little stars and get ready for a night of wonder and excitem...
13/01/2025

Kiddies Movie Night: A Magical Adventure Awaits!

Gather your little stars and get ready for a night of wonder and excitement at Amaryllis Hotel!

Event Details:
- Date: 15th January 2025
- Arrival Time: 5:30pm
- Venue: Amaryllis Hotel (Orchid)
- Admission: MK20,000 per child

Bring Along:
- Cozy blankie to snuggle up
- Favorite pillow for ultimate comfort
- Soft toy companion to share the magic

Enjoy:
- Delicious snacks and refreshing drinks to fuel the fun

Book Your Spot Today!

12/01/2025

Diso La Nzika

 Mtsogoleri wa Salvation For All  Ministries International Apostle Clifford Kawinga alimbikitsa anthu kuchita ulimi wa n...
12/01/2025



Mtsogoleri wa Salvation For All Ministries International Apostle Clifford Kawinga alimbikitsa anthu kuchita ulimi wa nthilira ngati mbali imodzi yothana ndi mavuto anjala munyengo yomwe mvula sinagwe bwino.

Iwo anena izi pomwe amapereka uthenga wabwino wa mawu amulungu komanso thandizo la chakudya kwa mabanja oposa 4,000 m'dera la Senior Chief Malemia m'boma la Zomba.

Iwo ati, "tili ndi mitsinje yomwe ili ndi madzi oti tikhonza kugwiritsa ntchito pa ulimi wanthilira. Komanso ofunika kuti tipemphere kwa Mulungu kuti anthu athe kukhala ndi chisomo cha zipangizo chifukwa akhonza kukhala ndi madzi koma ngati alibe zipangizo ndiye kuti ndi mavutonso ena apadera".

Iwo alimbikisanso omwe ali ndi kuthekera kothandiza ena kuti atero mogwirizana ndi boma ngati mbali imodzi yochepetsa mavuto anjala m'dziko muno.

"Tikhala tikupitirizabe ntchito imeneyi chifukwa timafuna kutumikira anthu omwe ali ndi moyo. Tchalitchi ndi anthu ndipo akakhala kuti ali ndi njala ndiye kuti sitingawatumikire moyenera". Atero a Kawinga.

Olemba Bertha Chirwa.

Address

Blantyre

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Tuesday 09:00 - 17:00
Wednesday 09:00 - 17:00
Thursday 09:00 - 17:00
Friday 09:00 - 17:00
Saturday 09:00 - 17:00
Sunday 09:00 - 17:00

Telephone

00265999844266

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mibawa TV posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mibawa TV:

Videos

Share