Blantyre Synod Radio

Blantyre Synod Radio Proclaiming The Gospel Of Our LORD JESUS CHRIST SOUTHERN REGION: 91.1FM
CENTRAL REGION : 100.3FM
NORTHERN REGION: 103.5FM
EASTERN REGION : 88.6FM

Kambani a Malawi pa wailesi ya Blantyre Synod okupatsirani Emmanuel Harry (07:20am - 08:00am)Boma lati anthu pafupipafup...
27/12/2024

Kambani a Malawi pa wailesi ya Blantyre Synod okupatsirani Emmanuel Harry (07:20am - 08:00am)

Boma lati anthu pafupipafupi 1 million nyumba zawo zilumikizidwa magetsi kudzera mu ntchito yomwe ikutchedwa Ascent 2.

Nduna yoona za mphamvu ndi magetsi Ibrahim Matola yati ntchitoyi igwiridwa ndi thandizo la ndalama pafupipafupi 424 billion kwacha zomwe dziko la Malawi kudzera ku bungwe la ESCOM lalandira kudzera ku Bank yaikulu pa dziko lonse ya World Bank.

Poikirapo ndemanga mkulu wa bungwe la anthu ogula la Consumers Association of Malawi CAMA John Kapito wati ntchitoyi ithandiza anthu ochuluka kuti apeze magetsi mosabvuta.

Kapito wati ngakhale ili nkhani yabwino koma nkofunika kulingalira zowonjezera mphamvu magetsi m'dziko muno pofuna kuthana ndi bvuto lakuthimathima kwa magetsi.

Nkhaniyi mwailandira bwanji?

Tipatseni ndemanga yanu.

Imbani foni pa: 0885513399 kapena 0984425156

Tumizani uthenga wa m'manja ku: 0885205184

Phungu wa nyumba ya malamulo wa dera la Mulanje - Limbuli Daudi Chida wati ndiwozipereka kusintha miyoyo ya achinyamata ...
22/12/2024

Phungu wa nyumba ya malamulo wa dera la Mulanje - Limbuli Daudi Chida wati ndiwozipereka kusintha miyoyo ya achinyamata a m'dera lake.

Chida yemwe ndi wachipani cha Democratic Progressive DPP walankhula izi lamulungu masana pamapeto pa chikho cha ndalama Zokwana K6.5 million ku Muloza m'bomali.

Iye wati anakhazikitsa chikhochi ndi cholinga chowapatsa achinyamata zochita kuti aleke m'chitidwe woipa womwe ungaike moyo wao pachiopsyezo.

Malinganana ndi phunguyu masewerowa agwira ntchito yaikulu yoiwalitsa mabvuto a namondwe Freddy amene anasakaza m'bali yaikulu ya dera la Muloza komanso apereka danga ku matimu a Ntopwa komanso Bangwe All Stars omwe atenga asungwana angapo a mpira wamiyendo kudzera mu mpikisanowu.

Polankhulapo mfumu yaikulu Njema ya yomwe inali mlendo olemekezeka yamema anthu kuti awonetse chikondi pa phunguyu pozamusankhanso kuti apitilire kubweretsa zitukuko komanso chimwemwe pakati pa achinyamata am'derali.

Timu ya Manyamba FC ndi inakhala akatswiri a ligiyi ku mbali ya Mpira wamiyendo wa Anyamata pomwe Gawani FC inachita bwino ku mpira wamiyendo wa asungwana.

Evidence Action has expressed concern over the tendency of some politicians and other electoral stakeholders to use chlo...
22/12/2024

Evidence Action has expressed concern over the tendency of some politicians and other electoral stakeholders to use chlorine dispensers under its Safe Water Now program for political messaging.

The Programs Manager for Safe Water Now, Moses Chisangwala, highlighted this issue on Saturday during the second day of the Southern Region Press Club Annual General Meeting in Mangochi.

Chisangwala stated that such actions are undermining efforts to improve access to safe water, especially in communities where politicians are using the dispensers as campaign tools and to disseminate voter process information ahead of the 2025 general elections.

He also noted an increase in vandalism of the dispensers in some communities and called for intensified civic education to foster mindset and behavior change among the public.

~Catherine Alumando ~

Presbytery ya Limbe pansi pa CCAP Blantyre Synod lamulungu yalandira m'busa Lyton Kilowe kukhala Moderator wa mpingo wa ...
22/12/2024

Presbytery ya Limbe pansi pa CCAP Blantyre Synod lamulungu yalandira m'busa Lyton Kilowe kukhala Moderator wa mpingo wa Mount Moriah CCAP.

Polankhula pa mwambo olandira m'busa Kilowe, yemwe anayimilira mlembi wa Presbytery ya Limbe M'busa Chifundo Chibaya walangiza a khristu a mpingowu kuti akhale okonda m'busa wao kuti akule ku moyo wa uzimu komanso wathupi.

Mlembi wa Mpingo wa Mount Moriah Harley Suliani anati kumbali yawo ayesetsa kukonza ubale wabwino ndi a busa awo atsopanowa ndicholinga chofuna kukwanilitsa masophenya omwe mpingo uli nawo.

Asanabwere pa mpingowu m'busa Kilowe anatumikiraponso mipingo ina monga Sakalawe, Nansengwe komanso Ndirande Kachere CCAP.

Limbe presbytery ya CCAP Blantyre Synod lero yakhazikitsa mbusa Victor Saidi Phiri kukhala moderator wa mpingo wa St. Co...
22/12/2024

Limbe presbytery ya CCAP Blantyre Synod lero yakhazikitsa mbusa Victor Saidi Phiri kukhala moderator wa mpingo wa St. Columba CCAP.

Mbusa Saidi Phiri wati ndiokonzeka kutumikira Mulungu pa mpingo wa St. Columba CCAP.

Ndipo m'malo mwa presbytery ya Limbe mbusa Mwachumu anati presbytery Yao ndiokondwa kukhazikitsa mbusa Saidi Phiri pa St. Columba CCAP ndipo akukhulupirira kuti mpingo'wu awutumikira bwino.

Iye wapempha akhristu apa St. Columba kuti aendere limodzi ndi moderator wao mbusa Saidi Phiri.

...

Mpingo wa Ndirande CCAP lero masana'wu unali ndi mwambo oimba nyimbo zokumbukira kubadwa Kwa Yesu Khristu.Mwambo'wu unac...
22/12/2024

Mpingo wa Ndirande CCAP lero masana'wu unali ndi mwambo oimba nyimbo zokumbukira kubadwa Kwa Yesu Khristu.

Mwambo'wu unachitikira pa mpingo wa Ndirande CCAP ndipo unatsogozedwa ndi moderator wa mpingo'wu mbusa Maxwell Ngwaya.

Mbusa Ngwaya analimbikitsa mpingo onse kuti uyamikire Mulungu kudzera mu nyimbo kamba kakubadwa Kwa Yesu Khristu kudzapulumutsa dziko lapansi

Pamwambo'wu panali makwaya onse a mpingo wa Ndirande CCAP amene onse anayimba nyimbo zokumbukira kubadwa Kwa Yesu Khristu.

...

Mbusa Colin Leman Mbawa amene amatumikira pa mpingo wa St. Peters CCAP mu Blantyre City Presbytery wapuma pa utumiki wak...
22/12/2024

Mbusa Colin Leman Mbawa amene amatumikira pa mpingo wa St. Peters CCAP mu Blantyre City Presbytery wapuma pa utumiki wake atatumikira zaka 21.

Mwambo okondwerera utumiki wa mbusa Mbawa unachitika lero pa mpingo wa St. Peters Ku Sigeregere mu mzinda wa Blantyre.

Pa mwambo'wu panali mthumwi zochokera Ku CCAP General Assembly, CCAP Blantyre Synod komanso Blantyre city Presbytery.

M'mau ake wachiwiri Kwa mlembi wamkulu wa CCAP General Assembly mbusa Dr. Getrude Kapuma anati mbusa Mbawa wachita zazikulu Ku general assembly maka pamene anali mlembi wamkulu wa Assembly'yi.

Ndipo m'mau ake m'malo mwa Blantyre city Presbytery mbusa Dr. Dennis Mulele anati mbusa Mbawa anali mbusa amene anali ndi mphatso yodziwa kutolera chuma chochitira chitikuko cha mmipingo imene amatumikira.

Mbusa Mbawa watumikira mmipingo monga Namatete CCAP, Zomba CCAP, St. Andrews CCAP komanso St. Peters CCAP.

...

Abambo asanu lero apatulidwa kulowa mu utumiki wa abambo pa mpingo wa Kabula CCAP mu Blantyre City Presbytery.Mkulu wa u...
22/12/2024

Abambo asanu lero apatulidwa kulowa mu utumiki wa abambo pa mpingo wa Kabula CCAP mu Blantyre City Presbytery.

Mkulu wa utumiki wa abambo mu CCAP Blantyre Synod mbusa Moses Chitao ndi amene wapatula abambo'wa ndi langizo kuti akhale abambo a chilungamo m'mabanja mwao komanso Ku mpingo kwao.

Mu ulaliki wake Mbusa Chitao anapereka chitsanzo cha Yosefe amene anali pa ubwenzi ndi Maria pamene uthenga wakubadwa Kwa Yesu unafika. Yosefe sanasuthike Koma kukhalabe munthu olungama.

Moderator wa mpingo wa Kabula mbusa Alex Jambo anati ndiokondwa kuti utumiki wa abambo pa Kabula ukukula kwambiri ndipo anati akuyembekezera abambo ena kulowa mu utumiki'wu.

...

Mabungwe siaboma omwe amatenga nawo gawo pa nkhani za chisankho apempha bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), kut...
19/12/2024

Mabungwe siaboma omwe amatenga nawo gawo pa nkhani za chisankho apempha bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), kuti libwereze kalembera wachisankho m'magawo onse atatu.

Izi zalankhulidwa pa mkumano womwe mabungwewa anakonza mu mzinda wa Blantyre wochita kauniuni m'mene kalembera wachisankho wayendera.

Mkulu woyan'ganira ntchito za bungwe la National Initiative for Civic Education (NICE) m'boma la Blantyre, Glory Ngosi Maulidi wati mkumanowu wamanga chimodzi kuti kalembera wachisankho abwerezedwe kutsatira zotsamwitsa zingapo monga kulephera kwa anthu kupita kukalembetsa zomwe zinakhuzanso anthu omwe ali ndi chiphaso chaunzika omwe ena mwa iwo sanalembetse mkaundulayu.

Maulidi wati wapempha mabungwe onse akukhuzidwa pa ntchitoyi kuti agwire ntchito limodzi polimbikitsa anthu kuteteza ziphatso zawo kuti azakwanitse kuponya voti chaka cha mawa.

Polankhulapo, Praise Mwenegamba m'modzi mwa akuluakulu a bungwe la Institute for Policy Interaction (IPI) lomwe linali nawo pa nkumanowu wati bungwe la National Registration Bureau (NRB) linalephera kubweretsa zipangizo zawo zomwe zinachititsa kuti anthu ambiri alephere kulembetsa nkaundula wa voti.

Mwenegamba wati pempholi ndi mbali imodzi yowonetsetsa kuti chisankho chizakhale chopanda mpungwepungwe kamba ka mphekesera zosiyanasiyana pa nkhani ya kulephera kwa mabungwe a MEC komanso NRB kogwira ntchito yao moyenera.

18/12/2024

Mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera wati maulendo amene wakhala akuyenda kupita kunja kwa dziko lino akhala akuchitika mogwirizana ndi ndondomeko zosamalira chuma chadziko lino.

Chakwera wati maulendowa ambiri akhala akukonzedwa komanso kulipililidwa ndi maikowo.

Mtsogoleriyu wayankhula izi kunyumba ya malamulo poyankha funso lochokera kwa mtsogoleri wa mbali yotsutsa boma Dr. George Chaponda amene amafuna kudziwa njira zimene boma likutsatira kukonza chuma chadziko lino.

The Ministry of Education is working on a Higher Education Overarching Bill, which seeks to address gaps in tertiary edu...
18/12/2024

The Ministry of Education is working on a Higher Education Overarching Bill, which seeks to address gaps in tertiary education, including protecting students from enrolling in unaccredited programs.

The Secretary for Education, Professor Mangani Chilala Katundu, revealed this on Tuesday during a Stakeholders' Consultative Meeting in Dowa.

He added that the bill will enable the Ministry to effectively conduct audits on programs being implemented in both public and private universities. This will, in turn, help regulate and penalize those who contravene the stipulations of the act.

Katundu also stated that the bill will empower the National Council for Higher Education (NCHE) to address issues of individuals obtaining academic titles without completing the required studies, a malpractice that will be criminalized.

~Catherine Alumando~

Kambani a Malawi pa Wailesi ya Blantyre Synod okupatsirani Emmanuel Harry komanso Eunice Mmwala (07:20am - 08:00am)Kafuk...
18/12/2024

Kambani a Malawi pa Wailesi ya Blantyre Synod okupatsirani Emmanuel Harry komanso Eunice Mmwala (07:20am - 08:00am)

Kafukufuku wa mabungwe anayi omwe akutchedwa ndi dzina loti Chisankho Watch wapeza kuti atsogoleri ena a zipani zandale amapeleka ndalama kwa anthu ogwira ntchito ku bungwe la Malawi Electoral Commission mu gawo lachitatu la kalembera wa voti lomwe linatha sabata yatha pa Lachinayi sabata pa 11 December 2024.

Bungweli lalankhula izi pamene nthambi zosiyanasiyana zikuunikila momwe ntchito yolemba anthu mukaundula wa voti wagawoli wayendela.

Polankhula pa msonkhano wa atolankhani dzulo, m'modzi mwa akuluakulu a bungwe limeneli Bishop Gifford Matonga wati mwachitsanzo phungu wina anapeleka ndalama zokwana K10,000 kwa anthu ogwira ntchito a MEC wa pa zifukwa zomwe sizikudziwika zomwe akukuganiza kuti zitha kusokoneza ntchito yakalembera komanso zisankho za chaka cha mawa.

Nkhaniyi mwailandira bwanji?

Nthambi zokhuzidwa komanso zipani za ndale zichite motani kuti m'chitidwe umenewu utheretu pamenenso pali kuthekera kobwereza kalembelayu mu gawo loyamba ndi lachiwiri.

Text Line: 0885205184
Call Line: 0885513399/0984425156

Bank ya First Capital mogwirizana ndi bungwe loyan'ganira masewero a mpira wamiyendo achisodzera m'dziko muno la Nationa...
17/12/2024

Bank ya First Capital mogwirizana ndi bungwe loyan'ganira masewero a mpira wamiyendo achisodzera m'dziko muno la National Youth Football Association yapereka thandizo la zipangizo zophunzilira ku sukulu yophunzitsa ndi kusamallira ana amasiye ya SOS Childrens Village mu mzinda wa Mzuzu.

Malingana mkulu woyan'ganira za malonda ku bank'yi Twikale Chirwa iyi ndi njira imodzi yopititsa patsogolo maphunziro komanso kulimbikitsa ophunzira.

Chirwa wati kutengera kuti ophunzira amenewa ndi ogwira ntchito a mawa anachiona cha nzeru kuti limodzi ndi bungwe la NYFA agwire limodzi ntchitoyi.

Polankhulapo atapereka thandizoli, wapampando wa bungwe la NYFA Tiyenkhu Chavula wati iyi ndi ntchito yomwe imagwiridwa chaka ndi chaka makamaka ligi ya First Capital ikamapita kumapeto.

Chavula wati anasankha kuzapereka thandizoli chifukwa sukuluyi imasunga ana aulumali omwe akukumana ndi mabvuto osiyanasiyana pa maphunziro awo tsiku ndi tsiku.

Sukulu zina za sekondale zomwe zapindula ndi thandizoli ndi Mzuzu Government Chibavi komanso Mchengautuwa.

Katundu yemwe waperekedwa ndi wa ndalama zokwana K1 million kwacha.

Zithunzi: First Capital Bank

Kambani a Malawi pa Wailesi ya Blantyre Synod okupatsirani Emmanuel Harry komanso Eunice Mmwala (07:20am - 08:00am)Malip...
17/12/2024

Kambani a Malawi pa Wailesi ya Blantyre Synod okupatsirani Emmanuel Harry komanso Eunice Mmwala (07:20am - 08:00am)

Malipoti akuonetsa kuti a Malawi omwe anafunitsitsa kulembetsa nkaundula wa voti pa tsiku lomwe kulembetsa kumapita kumapeto sabata yatha analephera kutero chifukwa makina a bungwe la MEC anasiya kugwira ntchito.

Mneneli wa bungwe la MEC Richard Mveriwa watsimikiza zankhaniyi.

Iye wati bungwe la MEC lili mkati mofuna kuona chitsogolo ndipo litulutsa bwino lomwe zomwe lichite pa nkhaniyi.

Malipoti akuti makina a bungweli anasiya kugwira ntchito m'mene nthawi imati 4 koloko madzulo anthu ali pa mzere wofuna kulembetsa nkaundula wa votiyu.

Nkhaniyi mwailandira bwanji?

Tiuzeni chiyembekezo chanu kuchokera ku bungwe la MEC

Text Line: 0885205184
Call Line: 0885513399/0984425156

Self Help Africa a non-profit making organization says over 1000 households are using chitetezo mbaula in Chiradzulu dis...
16/12/2024

Self Help Africa a non-profit making organization says over 1000 households are using chitetezo mbaula in Chiradzulu district.

The organization's project coordinator Issah Bakili said this at the end of the football bonanza held at Chiradzulu Secondary School ground yesterday.

Bakili said they are happy to have reached its target of convincing people to adopt new ways of cooking through chitetezo Mbaula than the old ways which require more firewood.

He said sporting activities football in particular, people who were educated on how best ways they can conserve and protect the environment.

He added that selling Chitetezo Mbaula at a price of one thousand five hundred kwacha also contributed to their success.

The organization will in January next year shift its attention to Mulanje and Phalombe districts where people will be told the same.

In the final match, Gande FC emerged winners after a massive two nil victory over Sniper Socials team.

Veritas college Malawi yapereka ma certificate Kwa akhristu 46 amene atsiriza maphunziro a Veritas module 1 komanso modu...
15/12/2024

Veritas college Malawi yapereka ma certificate Kwa akhristu 46 amene atsiriza maphunziro a Veritas module 1 komanso module 2 pa mpingo wa Nancholi CCAP mu presbytery ya Blantyre City.

Mwambo'wu unatsogozedwa ndi moderator wa mpingo wa Nancholi CCAP mbusa Davidson Moyo amenenso ndi mkulu wa nthambi yolalika mau a Mulungu mu CCAP Blantyre Synod ya Missions, Evangelism and Training.

Mmawu ake mbusa Moyo wawalimbikitsa akhristu'wa kuti akachite zimene aphunzira komanso kuti asasiyire maphunziro'wa panjira.

Mwa onse amene alandira ma certificate 23 amaliza module 1 ndipo 23 amaliza module 2.

.....

Presbytery ya Blantyre city mu CCAP Blantyre Synod lero yakhazikitsa mbusa Johnson Damalekani kukhala moderator wa mping...
15/12/2024

Presbytery ya Blantyre city mu CCAP Blantyre Synod lero yakhazikitsa mbusa Johnson Damalekani kukhala moderator wa mpingo wa Mbawa CCAP.

Mwambo okhazikitsa mbusa Damalekani unatsogozedwa ndi moderator wa Blantyre City Presbytery mbusa McDonald Siliya.

Pamwambo'wu panali wachiwiri Kwa Moderator wa CCAP Blantyre Synod mbusa Annie Kapinda, komanso abusa osiyanasiyana kuchokera mmipingo ya CCAP Blantyre synod, mafumu, komanso akhristu.

Mkulalika kwake wachiwiri Kwa Moderator wa Blantyre City Presbytery Mbusa Felix Kuombola anati munthu aliyense kuphatikizapo atsogoleri a mpingo ndi dziko akuyenera kuchita cholinga chimene Mulungu anawaikira pa Malo amene ali.

Mlendo olemekezeka pa mwambo'wu anali mtsogoleri wa chipani cha PDP Kondwani Nankhumwa.

....

Chipani cha  United Transformation movement UTM, chasankha mai Patricia Kaliati kukhala mlangizi wa chipanichi pa nkhani...
14/12/2024

Chipani cha United Transformation movement UTM, chasankha mai Patricia Kaliati kukhala mlangizi wa chipanichi pa nkhani zandale ndi ntchito zokopa anthu.

Mlembi wamkulu wa chipanichi Willet Kalonga watsimikiza za kusankhidwa kwa a Kaliati m'chikalata chomwe chipanichi chatulutsa.

Kalonga wati chipanichi chasankhanso a George Saonda ngati regional governor wachipanichi mchigawo chakumwera.

Iye wati awiriwa ayamba ntchito yawo .

Kaliati yemwe anapikisana nawo pa mpando wa mtsogolleri wa chipanichi adagwa kuzisankho zomwe zinachitika ku Mzuzu mwezi wapitawo.

Address

The Station Manager Po Box 413
Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Blantyre Synod Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Blantyre Synod Radio:

Videos

Share