Umoyo FM Community Radio Station

Umoyo FM Community Radio Station Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Umoyo FM Community Radio Station, Radio Station, Saiti kadzuwa, Mangochi.

16/01/2025

Bungwe la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR) lapempha anthu kuti apewe kuchitila nkhanza anthu okalamba komanso anthu achialubino.

Bungweli lidakonza masewero ampira wa miyendo komanso ntchembele mbayi ndicholinga chofuna kufalitsa uthengawu ndipo mwambowu unachitika lachiwiri, pa 14 January 2025 pa bwalo la zamasewero la Mpondas CDSS m'boma la Mangochi
Polankhula ndi wailesi ino mkulu wa bungweli a Micheal Kaiyasa adati anagwilitsa ntchito masewerowa ngati njila imodzi yopelekela uthenga wawo umene umalunjika kunkhanza zimene anthuwa akukumana nazo.

A Kaiyatsa anati, anthu achikulire akuzuzidwa powaganizira kuti ndi afiti zomwe zikuzetsa nkhanza zosyanasyana monga kuthamangitsidwa kudera, kumenyedwa komanso kuphedwa kumene, zomwe zikubweletsa mantha pakati anthu achikulilewa.

Iwo adatinso miyoyo ya anthu achi alubino imakhala pachiopsezo maka mu chaka cha pamene chisankho chayandikira, pamene anthu ena amakhulupilira kuti mafupa awo amathandizira kuchitila zinthu zina zosyanasyana zamasenga ndipo izi zimayika miyoyo yawo pachiopsezo.

A Kayiyatsa adatinso mkofunika kuti anthu akhale ndi udindo kuti afalitse uthenga komanso poonetsetsa kuti anthu okalamba komanso achialubinono akukhala momasuka mdera mwawo.

Pothilirapo ndemanga sub-T/A Mambo adayamikila bungwe la CHRR chifukwa cha uthenga omwe adawabweretsera ponena kuti ndiofunika kwambiri mdera lawo.
Muchaka chapitachi anthu 18 achikulire aphedwa kamba kowaganizira kuti ndi afiti.

Timu yampira wa miyendo ya Mpondas United inagonjetsa team ya Kalonga Stars 4 kwa 2 kuzera kumapenate pamene mpila wa ntchembere mbaye timu ya Kalonga Sisters inagojetsa Mpondas United Sisters ndi mabasiketi 19 kwa 14.

Bungwe la CHRR lili pa ntchito yodziwitsa anthu za kuyipa kochitila nkhanza anthu achikulire komanso achialubino, mu project yotchedwa “ strength minority rights ‘’ ndipo ikugwira mothandizana ndi bungwe la CEDEP ndithandizo la ndalama kuchokera ku Royal Norwegian Embassy
By Brian Nkonde

09/01/2025

Nthambi yoona zakusintha kwa nyengo dziko muno yati Namondwe otchedwa Dikeledi wabuka panyanja yamchere ya Indian.

Malinga ndi nthambiyi,Namondweyu akuti akulowera mudziko la Mozambique.

Pakadali pano, nthambiyi yati ikulondoloza mwa chidwi pamomwe namondweyu akuyendera.

Wolemba :Francis Chitseko

.8Mhz

Ngati njira imodzi yokonzekera zisankho za chaka chino limodzi mwa bungwe lomwe limalimbikitsa mtendere m'dziko muno la ...
09/01/2025

Ngati njira imodzi yokonzekera zisankho za chaka chino limodzi mwa bungwe lomwe limalimbikitsa mtendere m'dziko muno la Centre for Social Concern lakonza maphunziro apadera kwa atolankhani a zisankho.

Maphunzilowa akulunjika pa ukadaulo wofalitsa nkhani moyenera mu nyengo ya zisankho.

Potsekulula zochitikazi amene amaona za zochitika za ma program ku bungwe la Centre for Social Concern Tobias Jere wapempha atengambali onse kukhala ndi chidwi. Iwo ati ndi khumbo lao kuti atolankhani adzagwire bwino ntchito Munthali ya zisankho pakuti anthu amadalila uthenga wao.

Maphunzirowa amene aitana atolankhani kuchokera nyumba zofalitsa nkhani zosiyanasiyana Ukuchitikira Ku Holiday Motel m'boma la Mangochi ndipo achitika kwa masiku awiri.

Wolemba :Macklove Mafuta.

.8Mhz

09/01/2025

Apolisi m'boma la Mangochi atsekera mchitokosi mayi wina wa zaka 26, Chrissy Paulo yemwe akumuganizira mlandu ovulaza mamuna wake pomudula chala.

Malingana ndi wofalitsa nkhani za apolice ya Mangochi Inspector Amina Daudi, mayiyu anachita izi pa doko la Makawa m'bomalo atampeza mamuna wakeyo akuchezetsa akazi ena.

Pali chikayiko choti Mayiyu anachitira nkhanza mamuna wakeyu kamba ka nsanje ndipo pakadali pano mayiyu akuyankha mlandu ovulaza munthu, m'bwalo la First Grade Magistrate.

Paulo ndi wochokera m'mudzi mwa Makawa m'dera la mfumu yayikulu Mponda,M'boma la Mangochi

.8Mhz

05/01/2025

Bambo wina wadzipha pamalo ena ogona alendo m’tauni ya Mangochi atamwa mankhwala ophera tizilombo.

Ofalitsa nkhani pa police ya Mangochi inspector Amina Tepani Daudi wauza Umoyo FM kuti womwalirayo, yemwe sakudziwika dzina lake koma akuganizilidwa kuti ndi wa a 30 za kubadwa ndi wochepa thupi, wakuda, komanso ali ndi ndevu zapakatikati.

Malinga ndi Daudi, woyang'anira pamalopa wati bamboyo anabwera yekha madzulo a pa 3 Januware 2025 ndipo Anawonedwa komaliza atanyamula botolo la mowa ndi jumbo lapulasitiki lakuda.

"Mmawa wotsatira, wogwira ntchito pa malowa anagogoda pachitseko chomwe anagona mkuluyu kangapo kuti akakonzemo mwachizolowezi koma sanayankhe ndipo patatha maola angapo, wokonza mchipidacho anatsegula chitseko mokakamiza kenako adapeza bamboyo ali chikomokere komanso ali ndi masanzi. Apolisi ofufuza omwe anafika pamalowa anapeza bamboyo atavala kabudula wa mkati yekha, ali ndi botolo lopanda kanthu la mowa wa Kuche Kuche komanso mankhwala ophera tizilombo a Snowstorm." Anatelo Daudi.

Zotsatira zachipatala zatsimikitsa kuti imfa ya mkuluyu inabwera chifukwa chomwa mankhwala ophera tizilombo mosakanikirana ndi mowa.

Padakali pano thupilo likusungidwa kumalo achisoni a chipatalachi podikirira kuti achibale adziwike.

.8Mhz.

Apolisi m’boma la Mangochi amanga amayi atatu omwe akuwaganizira kuti amaba   mafuta ndi zinthu zina za  m’msitolo ya Ch...
02/01/2025

Apolisi m’boma la Mangochi amanga amayi atatu omwe akuwaganizira kuti amaba mafuta ndi zinthu zina za m’msitolo ya Chipiku m’bomalo.

Anthuwa ndi a Daina Thukuwa, azaka 60 zakubadwa womwe anamagidwaposo m'mbuyomu pa mlandu ngati omwewu, a Rose Samson, azaka 66 za kubadwa ndi a Lucy Mangani, azaka 64 zakubadwa.

Malingana ndi Inspector Daudi pa 2 January , 2025, atatuwa adalowa kumalo osungira katundu mu sitolo ya Chipiku ngati makasitomala. Iwo akuti adabisa zinthu zomwe adabazo, kuphatikizapo zigubu zitatu za mafuta agalimoto zokwana malita asanu.

Wogwira ntchito m’sitoloyo anayamba kukayikira ataona mmene amayendera modabwitsa, zomwe zinawachititsa mantha ndi kuwachita chipikishen.

Oganiziridwawo akuimbidwa mlandu wakuba, motsutsana ndi gawo 278 la malamulo ndipo anthuwa akuyembekezeka kukaonekera kubwalo lamilandu kafukufuku yense akatha.

.8Mhz

Apolisi m’boma la Mangochi apempha asodzi kuti azitsatira kwambiri zonena za owona za nyengo kuti apewe ngozi.  Izi zadz...
02/01/2025

Apolisi m’boma la Mangochi apempha asodzi kuti azitsatira kwambiri zonena za owona za nyengo kuti apewe ngozi.

Izi zadza kamba ka imfa ya asodzi awiri omwe amwalira atawombedwa ndi mphenzi pomwe amachita usodzi ku nyanja ya Malawi dela la Moto.

Wolankhulila polisi ya Mangochi, Inspector Amina Tepani Daudi, wauza wayilesi ya Umoyo kuti izi zinachitika madzulo a pa 31 December 2024 m’dera la mfumu yayikulu Namabvi m’bomalo.

Awiriwa Ndi Adam Paudala, 25, wa mmudzi mwa Ng’ombe , mfumu yayikulu Namabvi ku Mangochi, Ndi Mark Nedi, azaka 20, ochokekera mmudzi mwa Mwanapiye, mfumu yayikulu Mwambo ku Zomba.

“Asodzi asanu ndi atatuwa adapita kukasodza madzulo a tsikulo pogwiritsa ntchito mabwato awiri, bwato lililonse lidanyamula anthu anayi. Ali mkati mosodza. Mwadzidzi mphezi idaomba bwato limodzi. izi zinachititsa kuti bwato lionongeke Ndi kupha amuna awiriwa." Daudi anatero.

Asodzi onse anayi amene anali m’botimo anagwera m’madzi. Pomwe awiri adapulumutsidwa ndi anzawo m'bwato lachiwiri, Paudala ndi Nedi adamira ndikusowa.

Zotsatila zachipatala cha Lungwena Health Centre ndizo zidatsimikiza kuti adamwalila ndi moto wa mphanvu ya chiphaliwali.

Wolemba :Victoria Solijala

.8Mhz.

Umoyo FM ingathe kutsimikiza za kuchotsedwa kwa Dr Michael Usi mchipani cha UTM. Izi ndi malingana ndi kalata yomwe chip...
31/12/2024

Umoyo FM ingathe kutsimikiza za kuchotsedwa kwa Dr Michael Usi mchipani cha UTM.

Izi ndi malingana ndi kalata yomwe chipanichi chatulutsa chosayinidwa ndi a Felix Njawala amene ndi mlembi wamkulu wa chipanichi.

A Dr Usi anawaitana ku komitiyi kuti akayankhe mlandu ofuna kubweretsa chisokonezo mchipani omwe komitiyi ikuwazenga, koma iwo sadapite.

.8Mhz.

30/12/2024

Komiti yosungitsa mwambo mchipani cha UTM inali ndi mkumano womwe mwa zina unayitanitsa amene anali mtsogoleli wa chipanichi a Michael Usi.

Koma ku mkumanowu Dr Michael Usi amene amayendera anthu Madela a ku mmwera kwa dziko lino sanapezeke.

Mwa zina chipanichi chimafuna a Usi ayankhepo za zina zimene analankhula zimene akuti mzonyazitsa chipani.

Mneneri wa UTM, Felix Njawala wati izi sizinalepheretse mkumanowu ndipo apereka otsatila akamaliza kugundana mitu.

Masiku apitawa Dr Usi anapempha chipanichi kuti chibwere poyera ndi kulongosola momwe anayendetsera ndalama yokwana 61 million imene anapatsidwa ndi boma pa nthawi ya Malilo a Dr Saulos Chilima.

.8Mhz

Mpila uja wathatu. Timu ya Malawi ndi Zambia omwe osewera ake ndi omwe amkatumikira matimuwa kalekale  afanana mphamvu p...
28/12/2024

Mpila uja wathatu.

Timu ya Malawi ndi Zambia omwe osewera ake ndi omwe amkatumikira matimuwa kalekale afanana mphamvu posagoletsana chigoli chinachilichonse pabwalo la Bingu munzinda wa Lilongwe.

Ngakhale panali Mvula yochuluka mpilawo unaseweredwa.

.8Mhz

28/12/2024

Mpila wa osewera akale adziko la Zambia ndi Malawi uli mkati.

Padakali pano sadamwetsanepo Chigoli.

.8Mhz

Osewera mpira wa miyendo akale atimu ya dziko lino akukumana ndi osewera akale a timu ya Chipolopolo adziko la  Zambia m...
28/12/2024

Osewera mpira wa miyendo akale atimu ya dziko lino akukumana ndi osewera akale a timu ya Chipolopolo adziko la Zambia masana ano pa bwalo la Bingu mu mzinda wa Lilongwe.

Bwaloli kukufika anthu ngakhale nyengo ikuonetsa kuti kungathe kugwa mvula.

Timu ya Malawi yomwe imadziwika ndi dzina loti Flames iyamba ndi osewera awa

Simplex Nthala
Harry Nyirenda
James Sangala
Peter Mponda
Elvis Kafoteka
Emanuel Chipatala
Robert Ng'ambi
Joseph Kamwendo
Ernest Mtawali
Fischer Kondowe
Chiukepo Msowoya.

.8Mhz

 .8_MhzAs one way of making sure that the youths are refraining from the use of drug and substance abuse, Malawi Economi...
28/12/2024

.8_Mhz
As one way of making sure that the youths are refraining from the use of drug and substance abuse, Malawi Economic Justice Network (MEJN) organised a Bonanza with an aim of addressing the youths on harmful effects of drug and alcohol abuse.

A bonaza which date on Friday 27 December, 2024 at St Augustin 3 ground in Mangochi District, invited four teams from all T/A's where the project is being implemented under the theme ''Empowering young people (in and out of School Youths) to fight drug and alcohol Abuse''.

In an interview with the Programs Manager Cecelia Phiri said, the project will help the youths to free from any forms of abuse and alcohol and drug related harms, because sharp minded youths are good pillars in developing the country.

Phiri said the project has engaged different stakeholders from T/A, ADC level and District level so that the youth can be helped and they have put much effort to make sure that the issues to do with drug and alcohol abuse is stopped.

Commenting on the development Chairperson for Mangochi District Football Association (MDFA) Issa Brahim commended MEJN by saying that the massage they brought will help the youths not to be involved in drug and alcohol abuse which can lead them into bad behaviors.

It is a five year(2024-2028) project with support from NORAD Through Norwegian Church Aid (NCA) /Dutch Church Aid (DCA) and is being implemented in the four Traditional Authorities of Namkumba, Chimwala, Mponda, and Jalasi in Mangochi District and nationally (advocacy). It aims to raise awareness of the harmful effects of drug and alcohol abuse, with a strong focus on policy advocacy and community engagement.

By Brian Nkonde

28/12/2024

Apolisi ku Lilongwe amanga mkulu wina amene dzina lake ndi Blessings Jubani kamba kopezeka ndi ngaka (pangolin).

Polankhula ndi Umoyo FM mneneri wa polisi ya Lilongwe a Khumbo Sanyiwa ati a Jubani amangidwa pomwe apolisi amachita chipikisheni pa msika wa Kambanje.

Iwo ati a polisi anaimitsa njinga ya moto yomwe inanyamula anthu awiri ndipo modzi mwa iwo anali atanyamula chikwama chakuda.

"M'modzi mwa anthuwa ataona apolisiwa anataya chikwama chomwe ananyamula ndikuthawa. Izi zinachititsa kuti apolisiwa ayang'ane chomwe chinali mchikwamamo ndipo ndipomwe anapeza kuti ananyamula kanyama ka". Anatelo a Sanyiwa.

Padakali pano, apolisi apeleka ngakayi kwa oyang'anila nyama za nkhalango ndipo akuyembekezeka kuyankha mlandu opezeka ndi nyama yotetezedwa.

Wolemba :Iqra Adani.

.8Mhz

28/12/2024

Mwambo wamapemphero apadela okumbukira malemu Dr. Saulos Klaus Chilima uli mkati ku Nsipe Catholic, Parish ya Ntcheu.

Bambo Atanazio Manyeka ndi omwe akutsogolera mwambo wa nsembe ya misa yomwe anakonza ndi banja la a Chilima.

Banjali likukumbukiranso miyoyo ya abale onse omwe adamwalira.

Mtsogoleri wa chipani cha UTM Dr. Dalitso Kabambe ndi akuluakulu ena achipanichi ali nawo pa misa.

Dr. Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu adamwalira pa ngozi ya ndege pa 10 June, 2024 m’nkhalango ya Chikangawa.

Wolemba :Victoria Solijala.

.8Mhz

28/12/2024

Police in Mangochi have arrested Kefas Peter Kanyama, 51, for possession of unlicensed fi****ms and conduct likely to cause a breach of peace.

Public relations officer of Mangochi Police Station inspector Amina Tepani Daudi told Umoyo FM that Kanyama had been on the run since December 12, 2024, following a chaotic incident at the Koche Roadblock, where he fired two fi****ms into the air.

On the evening of the incident, Kanyama approached the checkpoint, driving a white Toyota Fortuner (registration NN 424) alone. He found two Liwonde police officers and Malawi Revenue Authority (MRA) officials on duty.

"Unexpectedly, Kanyama parked his vehicle, exited with a Greener rifle, and fired it into the air without provocation. He then retrieved a pistol from his car and discharged it again multiple times into the air. When confronted, Kanyama allegedly threatened to locate and shoot a certain Traffic Officer, who was not present at the time." Daudi said.

After his threats, the two officers attempted to arrest him but proved futile as he fled the scene in his car.

Manhunt was launched, on December 27, 2024, detectives spotted Kanyama’s vehicle within the township and swiftly apprehended him.

During the arrest, police recovered a Greener rifle loaded with one bullet and revolver pistol with ten live bullets in the vehicle. Kanyama failed to produce valid documents for the fi****ms.

Daudi assured that Kanyama is expected to appear in court to face charges leveled against him once the necessary documentation is finalized.

The suspect hails from Kuweruza Village, Traditional Authority Changata in Thyolo.

Reported by Victoria Solijala.

28/12/24

Pamene chiwerengero cha anthu omwalila kamba kodzipha chikululuka m'dziko muno, zadziwikano kuti ambiri mwa anthuwa akum...
28/12/2024

Pamene chiwerengero cha anthu omwalila kamba kodzipha chikululuka m'dziko muno, zadziwikano kuti ambiri mwa anthuwa akumakhala a bambo

Izi ndi malingana ndi Komishonala wa apolisi m'chigawo cha pakati ku m'mawa Rhoda Manjolo.

Malingana ndi commissioner Manjolo, m'chaka cha 2024 chiwerengero cha abambo omwe adzipha chakwera kwambiri poyelekeza ndi Chaka chatha.

Iwo amalankhula izi pa phwando lomwe linakonzedwa pa sukulu ya sekondale ya Loyola m'boma la Kasungu.

A Manjolo ati anthu onse omwe adzipha m'chakachi ndi 74 ndipo mwachiwerengelochi 64 ndi amuna ndipo 10 ndi akazi.

"Abambo ambiri akamakumana ndi mavuto ndipo sayankhula akakhala ndi nkhawa zomwe zikukolezera m'chitidwewu." Anatelo a Manjolo.

Kotero Iwo apempha a bambo kuti adziulula nkhawa zao kuti ena adziwathandiza kusiyana ndi kuchotsa moyo.

Mwambowu unachitika mwazina akukondwelera momwe agwilira ntchito m'chakachi.

Wolemba: Loice Gama.

.8Mhz

28/12/2024

Chiwerengero cha anthu othawa nkhondo imene ikuchitika m'dziko la Mozambique chikukwera m'dziko muno.

Padakali pano chafika pa 2,497 pa ma banja pafupifupi 2000.

Izi ndi Malingana ndi zomwe bwanamkubwa wa boma la Nsanje a Dominic Mwandira watsimikiza.

Nkhondoyi inayambika pamene khothi la m'dzikolo linagamula kuti a Daniel Francisco Chapo ndi amene anapambana pa zisankho zimene zinachitika mwezi wa October. Izi sizinasangalatse mtsogoleli wa RENAMO a Ossufo Momade.

Wolemba: Brian Nkonde.

.8Mhz.

Address

Saiti Kadzuwa
Mangochi
P.OBOX363

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Tuesday 09:00 - 17:00
Wednesday 09:00 - 17:00
Thursday 09:00 - 17:00
Friday 09:00 - 17:00
Saturday 09:00 - 17:00
Sunday 09:00 - 17:00

Telephone

+265882570759

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Umoyo FM Community Radio Station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Umoyo FM Community Radio Station:

Videos

Share

Category