Victor Creatives

Victor Creatives GRAPHIC DESIGN

SONG COVER
EP/ALBUM COVER
BIRTHDAY CARD
BUSINESS CARD
WEDDING CARD

30/01/2025

Mzimai wina amati akamapita ku nsika kogulisa matemba ndi tomato,amasamba mankhwala ena mkumangilira mchiuno wautali ku msika kogilisa.
Akatero amagulisa mwakathithi ndipo amati mankhwala awawa ndiogwira ntchito.
Tsiku lina anaiwala kusamba zitsambazo komanso kuika zina mchiuno nakumbukila ali mnjila ndipo anadandaula nati haaa lero sinkagulisa kwambiri ndapanga misteck.
Atayala matemba akewo,kunabwera munthu mmodzi naphatikiza malo onse amatembawo ndi tomato mkuzigula kamodzi nati kwathu kuli ulinamwali nampasa ndalama.
Apa mai uja anadabwa nati haaa zodabwisa ndithu ndagulisa zonse popanda kusamba mankhwala?mmawa ndiyesanso.
Kutacha tsiku lina anapita chomwecho ndipo anagulisa matemba onse nk*tha.
Mmawa lake anayesa kusamba ndikumangilira ena mankhwala mmchiuno koma atafika kunsika sanagulise olo themba limodzi.
Apa mai uja anazindikila k*ti ohhh!zonsezi ndi Mulungu kiti ndizigulisa kwambiri chomwe chija osati zitsamba ndimachedwa nazo zija eti?

Phunziro.
Chifukwa chokukonda kwambiri bwana wako kuntchito,usaganize k*ti ndika chithumwa waika mthumbako ayi koma Mulungu ndiye.
Chifukwa choyenda kwambiri business yako usaone ngati madzi a maliro ukusambawo ayi koma Mulungu ndiye.
Chifukwa chokukonda kwambiri mamuna wako m,banjamo osati khuzumule unamudyesayo ayi koma zik*tengera kufuna kwa Mulungu k*ti zako zizitheka nde tiyeni tisadalire zitsamba koma tidalire Mulungu muchina chilichonse ameniiiiii 🙏🙏🏼

KUIPA KOLONGOLOLA mayi wina Dela lina anali olongolola akafika pamalo khani inali kuyakhula yakhula ndipo anthu anafika ...
28/01/2025

KUIPA KOLONGOLOLA

mayi wina Dela lina anali olongolola akafika pamalo khani inali kuyakhula yakhula ndipo anthu anafika pomuzolowela mpaka kumupasa dzina k*t anabanda...............sikulina anabanda anapita kumalilo ndipo atafika kumalilo anayamba kulongolola amvekele malemuwa timkacheza nawo bwino kwambili ,ndiposo iiii anali amzanga koma thaw imeneyo tinalandana amuna tili ku primary school ____mpaka tinamenyana Ndipo eee malemuwa anandimenya kwambili moti eee anali aphamvu......anthu atamva anayamba kuseka ,Ali eee kod anabanda munali hule?____hehe iii,koma nabanda usandisekese Ndili pamalilo......ndipo anabanda anayamba kupitililizabe kuyakhula khani zambili pot anali amkamwa Ali eee koditu ku primary tapanga zinthu mpaka napangapo chibwenzi ndi aphunzitsi cholinga andikhonzese mayeso ,apa anthu anali kuseka ndithu Ali naba,timakuziwa bwino ndichifukwa chake pachinamwali chako amkanena k*t umapanga uhule tikulange? .....____anabanda anaseka hhehede eya mukuziwa tinali atsikana ma first crass sitimagawa kamba_______uku kunali kuchepa Kwa azimayi pamaliro

FUSO......kod makamba zandani mukakhalaguru? .....musakhale ngat anabanda olongolola mukakhala paguru koma khalani okamba zayesu thawi zonse monga ku Luka 24:13_35......timva khani ya kiliyopa ndimzake k*t panjila yopita ku emawo amkakamba zayesu yekhayekha _______mukakamakamba zayesu YESU AMAKHALA nanu pafupi mukamakamba zakudziko YESU amak*thawani.......kaya muli k*tchito,kaya ku business,kaya ndikuphwando ,musalole kukamba zinthu zosayenela pak*t ingakhale yoswa 1:8 akuchenjeza k*t buku lachilamulo lisachoke pakamwa panu .....kusonyeza k*t ife sitiyenela kukamba thabwala KAPENA khani zoduka mutu ayi chifukwa tili masiku akumapeto oti thaw zonse tiyenela KUKHALA osamalisa ,pomwe zanthu watisiya tizikhuzika k*t mawa ndife osati pamalilo kumakamba khani mpaka kuseka ayi pak*t ambuye akufuna thaw zonse tizililile tokha monga ananenela Ali pamtanda paja k*t zilileni nokha pak*t kwanga kwatha _____Amenii🙏🏼🙏🏼

23/01/2025

Big shout out to my newest top fans! Blessings Mcdonald, Belina Phili, Patuma Yakin, Meya Tembo, Christina Wa Mike Banda, Rosalia Kathumba

ANGLE OF LOVEEpisode 02Story done by Blessings Kayuni McDavisPangani like tsamba  lino k*ti nkhaniyi izikufikani mosavut...
20/01/2025

ANGLE OF LOVE
Episode 02
Story done by Blessings Kayuni McDavis

Pangani like tsamba lino k*ti nkhaniyi izikufikani mosavuta.

Shukulani anadikira mpaka phwando lidafika Ku mapeto ndipo pamene anthu ena anayamba kuweruka ndipo iye adapeza mpata okumana naye.....
"Hey Jessica!!" Shukulani adamuyitana mtsikana wina yemwe anali pomwe Victor ndi mnzake adakhala. Shukulani ankamuziwa Jessica kamba koti amakhala koyandikana komano awiriwa sankachezerana
Jessica atamva kuyitanako adavomera ndipo Shukulani adapita pamalopa
"Hy!" adapereka Moni kwa mnzake Jessica
"Hey bho?" Jessica adamupasa moni mnzakeyo
"Shuwa!!" Shukulani adayankha
Atayankha moteromu Jessica anakhala chete nkumamuyang'ana
"a-ah bwanji ukundiyang'ana moteromo!" Shukulani adayankhura mofuna kuyambisa macheza.
"Of course ndikudabwa kaya ndimaona ngati k*ti ukufuna kuyankhura zinazake potengera ndi m'mene unandiyitanira muja"
"Oh okay osazitengera kungoti anzanga apitapita kunyumba pomwe ineyo sindikufuna kupita ndeno ntakuwonani inuyo ndinaganiza zoti ndingokhala nanu pamodzi nanga ndingokhala ndekhandekha"
Jessica ankamuziwa Shukulani machitidwe ake. Anali munthu osakonda kucheza ndi anthu ndipo kukhala komwe amakhala mtsikanayu ankangogwirizana ndi Judith yekha
"Komano iweyo lero....."
"Oh ndizabhobo ngati ndasokoneza ndikhoza kubwerera pomwe ndinakhala!" Shukulani adayankhura akuyimilira
"Ooh ayinso it's okay!" Blessings chibwezi chake cha Jessica adayankhirako
"Jessica ndimaganiza Kuti ukumuziwa!?" Victor adayankhurakonso
"Eya timakhala Ku area imodzi actually ndi neba wanga!" Jessica adayankha monyinyirika pak*ti iye sanasangalatsidwe ndi kubwera kwa Shukulani pamalopa.
"Oh Jessica ndikuziwa sunasangalale m'mene ndafikira pano Koma sik*ti udandaule ineyo siwamaboza ngati anzizako aja ndizak*ti sindingakakunenere kwanu” Shukulani adayankhura moserewura
"a-ah anzizake ati amenewo, Jessica asakhale Kuti akunena achina Violet?" Blessings adafunsa modabwa
"Iwenso umawaziwa ndomwewo ndikale!" Shukulani adayankha mwamphamvu
"Wawona zomwe ndimakuwuza!?" Blessings adayankhura mwasiliyasi
"a-ah bwanjinso!?" Shukulani anayankhura modabwa
"Ndimamuwuza nthawi zambiri k*ti asiye kucheza ndi atsikana amene aja Koma samamva ayi"
"oh come on Bule, sizokoka nkhani apa ndi anzanga chabe basi! Komanso nditasiya kucheza ndi amene aja ndingamacheze ndindani ku area kwathu kuja"
"nanga iyeyu simunthu!?" Blessings adayankhura akuloza Shukulani
"ndaniyo ameneyo, zingatheke bwanji munthu waku high school azikacheza ndi munthu waku primary" Jessica adayankhura momunyoza mnzakeyo
"Haaaa!?" Victor anadabwa
"Uli Ku primary?" munyamatayu adafunsa modabwa ngakhale k*ti nkhope yake ikachita kuoneseratu k*ti amafuna aziseka.
"Eya! sitandade 7!" Shukulani adayankha m'tima uli m'malo
"Bwanji Pali vuto!?"
"Oh um- kungoti..." Victor adachita kachibwibwi kuli kusowa choyankhura
"samakonda sukulu ndipo chipanda makolo ake kumamuwumiriza bwezi atasiya kalekale ndeno munthu oteroyo ndingamacheze naye zichani?"
Jessica ankayankhura mawu owawisa m'tima mwadaladala n'cholinga choti Shukulani akanyasidwa athe kuchoka pamalopa Koma ayi ndithu Shukulani sizinkamukhuza nkonse. Mwachoncho anthuwa adangoyamba kucheza.

Atacheza mwakanthawi kunja kunagwa m'dima ndipo kenako Jessica adasanzika Kuti akufuna azipita
"Hey Jessica ndi past 7 tu ndeno uk*thamangira zichani" Blessings adafunsa
"Ayinso kungoti ndikufuna ndizingopita basi!"
"Komano mesa unanena k*ti makolo ako anapita Ku Bliz-burg ndipo abwera sabata yamawa?"
"Eya ndichoncho komano ineyo sinazowere kukhala Ku lodge mpaka nthawi zino moreover ogwira ena ntchito wkuno amziwana ndi amayi anga ndeno atati andiwone Kuno nthawi zino zikhoza kukandivuta kwathu"
"Oh okay nde bwanji tipite kunyumba kwathu!" Blessings adapereka ganizo
"Eya ndikuona ngati ndi maganizo abwino!!" Shukulani anali atangokhala chete nthawi yonse koma atangomva maganizo omwe Blessings adaturusa adayankhirako mwamphamvu poganiza Kuti imeneyo ndiye inali njira yokhayo yoti atha kupeza mpata oti athe kumukolera Victor
"Komano kodi mesa kuli muchimwene wako!?"
"Ayinso wanyamuka leroli kupita ku Hygra!" Blessings atayankha moteromu anthuwa adagwirizana zoti apite kunyumba kwawo kwa Blessings. adayimisa tax ndikukwera Victor adakhala pafupi Shukulani pamene Victor adakhala pafupi ndi bwezi lake Jessica.

Atafika kunyumba kwawo kwa Blessings, munyamatayu adatenga mowa
"Hey Bule ufuna kumwa mowa!?" Jessica adafunsa modabwa
"ayinso umenewu simowa Koma wine!" Atayankhura moteremu Victor pamodzi ndi Shukulani adaseka
"Ndeno mukuseka zichani ndalakwisa kufunsa!?" Jessica adayankhura moboweka
"Oh ayinso mulamu inuyo simunalakwise kanthu!!" Victor adayankhura akuseka
" Ndeno iweyo ndi mnzakoyo museka zichani!?"
"Oh Jessica usamakhale ngati mwana tawona wine simowa amwene!"
"Shukulani usanditore ndikuziwa kale zoti wine ndi mowa bambo anga amakonda kumwa zimenezi"
"a-ah come on beibs! ndeno ndi omwe adakuwuza Kuti wine ndi mowa?"
"ayinso Koma ndimangoziwa ndekha!"
"A-ah amenewo ndi maganizo ako chabe!" Victor adayankhura kenako ndkusekura botolo la mowalo. Adathira mumatambula anayi
Victor adatengapo tambula yake chimodzimodzinso Blessings. Anyamatawa atatenga matambulawo anadabwa kuona Kuti atsikanawa akungoyang'ana
"Hey guys bwanji mukhoza k*tengapo Kaya" Blessings adayankhura ndipo kenako adamuyang'ana Shukulani yemwe ankawoneka nditimantha
"Hey Shukulani ndek*ti iwenso sumamwa!"
"Angamwe bwanji munthu oti ngakhale juice owawasa samamwa!" Jessica adayankhirako
"a-ah Koma mesa umamuseka mnzako!" Victor adafunsa modabwa
"Ineso ndimadabwatuu!" Jessica adathiraponso ndemanga
'umenewu ndimwauyi okhawo oti ndikhoza kumasuka ndimuyanlhura Victor' Shukulani adaziyankhura m'tima kenako adatenga tambula yamowa ija
"wanena ndani zoti sindimamwa!" mtsikanayu atangoyankhura moteremu adagugudiza tambula yonseyo pakamodzi kumusiya aliyense kukamwa kuli yasa
"haaaaa!!" Victor anadabwa
"One kick!!"
"Wow superb!!" Blessings adayamikira
"Oh Wawona mnzakoyo wangomwa Ngati madzi!" Blessings adayankhura kwa Jessica. Ngakhale k*ti mtsikanayu (Jessica) adayesera kukanisisa kumwa Koma Anyamatawa adamuyankhura zoti mpaka analibenso kuchitira mwina Koma kungomwa.

Anthuwa adayamba kumwa mowa wawo kwinaku akumvera nyimbo nkumavina. Shukulani ankamwa kuposa anzake iye anali ndi maganizo ofuna kulezera mwachangu.

Atamwa mabotolo awiri Jessica adalezereratu mpaka kumakanika kuyenda mwachoncho Blessings adaganiza zomutengera kuchipinda chake Kuti akapume pamene Shukulani ndi Victor anali akumwabe.........IKUPITIRIRA

Osayiwala kuchita layiki, kusiya ndemanga komanso kupanga like tsambali.

Wasapu number #0894614165

ANGLE OF LOVEEpisode 01Story done by Blessings Kayuni McDavisPangani like tsamba lino k*ti nkhaniyi izikufikani mosavuta...
19/01/2025

ANGLE OF LOVE

Episode 01

Story done by Blessings Kayuni McDavis

Pangani like tsamba lino k*ti nkhaniyi izikufikani mosavuta.

Kodi munakwatirapo kapena muli pabanja ndi munthu oti simunali naye mu chikondi ndipo mumasakasaka njira zoti mumusiyire? Victor nayenso chimodzimodzi. Anatenga sipuni yazakudya ndikuyika mkamwa mwake kenako adaponya maso ake pa mkazi wake Shukulani, yemwe panthawiyi anali kudya ngati k*ti mwina wakhala chaka chatunthu osalawa chakudya. Mnyamatayu adatsonya kenako ndikusamba m’manja ndipo atatero adamukankhira mbale yake yazakudya mkazi wake

“a-ah Vic chikatere ndechani?” Shukulani anafunsa modabwa

“zikuonetsa k*ti uli ndi njala kwambiri ndeno ulhoza kudyanso zangazi” Victor anayankhura mokhala ngati akuserewura

“a-ah ndakuwuza k*ti ndikufuna zina!?” Shukulani anaziwa chifukwa chimene mwamuna akeyu anasiyira kudya

“Noo! but i can see tha...”

“oh pepani chingerezi chanucho ine ayi, ndeno umati bwaa!?"

“oh my gosh this idiot!” munyamatayu adaziyankhura moboweka

“ukatero wayankhura mawu ondinyoza koma sindikusamala chomwe ndikufuna ubwerere pa mpando wako udye chakudya chako. ineyo ndikafuna chakudya china ndipita ku khitchini kamba koti chiliko chambiri"

“oh really!?”

“chaa?”

“oh ambuye anyway, chabwino ngati uk*ti china chiriko ku khitchini ndek*ti zili bwino. Ndeno ukamaliza izizi utha kukatengannso zina”

“wayamba kundinyozanso sichoncho!?” Shukulani adasintha nkhope ndipo adakhala siliyasi

“ayinso sik*ti ndikunyoza komano ndikungoyankhura ndi m'mene zinthu zilili kaya”

“bwanji ndiwayimbire foni amayi!?” Shukulani atangofunsa moteromu Victor adachita mantha

“oh um- come on!”

“Eey....!"

ataturusa liwu la chingerezi Shukulani adamuduliza. Mtsikanayu ankadana kwambiri ndizoti mwamuna wakeyu azimulankhurira chingerezi. Shukulani sukulu sanafike patali anali atalekezeta sitandade 7 mwachoncho mwamuna wake akati azimuyankhurira chingerezi ankaganiza k*ti akungomunyoza

“oh pepani….!” Victor adabwerera pampando

“hey beib sik*ti mpaka ufike pamenepo tawona ndimangocheza kaya!” Victor adayankhura momunyengerera mkazi wakeyo

"Oh kucheza amatero?”

“okay chabwino ndikupepesa!”

“oh chabwino ndeno yamba kudya!”

“a-ah komatu ndizak*ti ndakhuta ndeno um-”

“oh chabwino zikuonesa k*ti sunasinthebe ndeno ndek*ti ndingowayimbira foni amayi n'kuwawuza k*ti ati mwana wanu pano wayamba kudya pang’ono akumangoodya sipuno imodzi ndkkukhuta”

Victor chongomva moteromu nthawi yomweyo adayamba kudya. Shukulani naye adangoseka cha m'tima kenako ndikupitiriza kumadya.

“you are totally evil!” Victor adaziyankura m’tima kumunena mkazi wakeyo akumuyang’ana ndi diso la nkhwenzure.

Awiriwa akudyabe, foni ya Victor idalira ndipo munyamtayu atawona yemwe amayimbayo adapeza Kuti anali mnzake Blessings

“Yes man!” adayiyankha

“Yah bro zatheka ayise!” mnzakeyu adayankhura mokweza ndipo zinkawonesa k*ti anali muchimwemwe chochuluka

“hey man come on what is it?" Victor adafunsa mwachidwi

“oh come on ayise ndizokhuzana ndi proposal tinapanga ija!"

"E-eya yatani?" Victor adafunsa mwatcheru

"Kukampani kuja kunabwera abwana atsopano ndeno nditaziwa ndinapitaso zana, ukumbukira muja ndimati ndikufuna ndipite ku Bliz-burg (mzinda omwe uli ku west Bebe')?"

"Eya!!"

"Ndizoti pamene paja ndimapita ku kampaniko ndipo ndinakayesera kulankhurana ndi abwana atsopanowo. Nditawafotokozera zambiri zokhudza project yathuyo anandiwuza Kuti andiyimbira foni. Ine ndimangowona Kuti mwina azenfeteza Koma apapa ndangopeza Kuti akundiyimbira foni ak*ti tipiteko akakumane ndi tonsefe"

Blessings atayankhura moteromu Victor samakhulupirira
"oh bro sizamacheza apa, ukuziwa sindili mu Judi yomacheza nkhani ngati iyi okay!!?"

"Oh come on bro! ndili siliyasi kaya, ndizak*ti zathekadi ngati sukukhulupilira dikira bdik*tumizira 'record' yomwe timalankhurana ndi munthuyo paja foni yanga imachita record ma calls"
Blessings anadula kaye foni ndikumutumizira Victor record yomwe amanenayo. Victor ngakhale k*ti adasimikizadi k*ti mnzakeyo amayankhura zowona Koma samakhulupirirabe k*ti pulani yomwe anali kuyifunisisa pamoyo wake onse ingangotheka ngati moteremu.

Munyamatayu anali atangolemba mayeso ake omaliza amu kilasi yomaliza ya ku sekondale. Ali mkati mwaholide zinapezeka Kuti wachimwisa Shukulani mtsikana yemwe sanali naye pa ubwezi. Shukulani panthawiyi nk*ti ali sitandade 7. Anali wankulu Koma vuto linali loti sanali n'chidwi ndi maphunziro ndipo iye ankafuna kusiya zomwe makolo ake samalola.

Adakumana ndi Victor koyambirira ku phwando lina lomwe lidachitika mu area yakomwe amakhalako (Blue hills district) yemwe chinali chibwezi cha Blessings mawonekedwe a munyamatayu adamudolora kwambiri ndipo sadachitire mwina koma kuyamba kumukodolakodola

"Hey bwanji ukumamuyang'ana munyamata wabwera ndi Bule uja moteromo?" Mnzake Judith adamufunsa Shukulani atawona ka mchitidwe kachilendoka mwa mnzakeyu

"Hey a gel ndisaname wandisangalasa kwambiri"

"a-a-ah ndeno ukuchita kuzitchipisa moteromo bwanji!?"

"Ndeno nditani munthu sakumandipasa oroko tchansi"

"Ndipo ndibwino ungosiya kulotako!"

"a-ah ukufuna utanthauze k*ti chani pamenepo!?" Shukulani anadabwa ndimalankhuridwe a mnzakeyu

"Ukuona angakhale ndi mpata oti akuyang'ane iweyo? Tawona akuphunzuratu ku Bliz-burg High School ndeno ukuganiza Kuti angasamale za iweyo chifukwa chani?"

"Zilibe ntchito zimenezo ine ndi okongola ndipo..."

"E-ey usayambekonso matama ako apa!" Judith adamuduliza mnzake kuyankhura

"Ukuona ngati k*ti anthu onse amatengeka ndi mawonekedwe? ayi ndithu komanso look sharp matters!"

"Oh usachite mpaka kundiyankhurira chingerezi chakocho apa!!"

"Wawona ndeno ukuona ngati ungathamangise bwanji mwamuna wa high school ngati ameneyo munthu oti kuwerenga sumatha"

"Zilibe ntchito zimenezo ayise!!"Shukulani adayankhura mosasamala

"Ooh zowona!?"

"Kapena ukukayika!?"

"Osatiso kukayika komano ndi chilungamo mwanunayo si level yako" atamuyankhura moteromu Shukulani adazimva ngati k*ti waphwekesedwa kwambiri chomwe chinali chinthu chimodzi chimene iye ankadana nacho. Munthu azimuyang'anira pansi

"Ukuziwa chani ineyo si wageli ngati iweyo komano iyiyi ndi tchalenji yanga kwa iweyo ngati sindipana ameneyo leroli ndek*ti si ineyo ndipo ndikulonjeza k*ti ndikupangira chirichonse chomwe ungafune"

"Owooo!?”

"Yaah!" Shukulani adayankha molimba mtima

"Usayambeso zakozo ndikuwuziretu Koma, mayi ako amandiyankhura daily ak*ti nfikulimbikise zamaphunziro ndeno pempho langa ndi limeneri ukangoti walephera kupamga zomwe wanenazo upita kusukulu"

"Ooh nangano zikatheka!?"

"Ndek*ti uzanena chomwe ukufuna"

"Okay deal!!"

Awiriwa atagwirizana Shukulani adayamba kusakasaka mpata oyankhurana ndi Victor. Munyamatayu patsikuli pafufupi atsikana onse omwe anali Ku phwandoli amamufira ndipo mpata oti nkukhala omasuka sumapezeka. Shukulani anadikira mpaka phwando lidafika Ku mapeto ndipo pamene anthu ena anayamba kuweruka ndipo iye adapeza mpata okumana naye.....IKUPITIRIRA

Osayiwala kuchita layiki, kusiya ndemanga komanso kupanga like tsambali.

Wasapu number #0894614165
' library©2025

AMOYO NDI OPOSA ZONSE PAZIKO LAPASIMunthu wina amagwila ganyo yopasila matope sikulina kuna bwela bwana wina Ali pa gali...
17/01/2025

AMOYO NDI OPOSA ZONSE PAZIKO LAPASI

Munthu wina amagwila ganyo yopasila matope sikulina kuna bwela bwana wina Ali pa galimoto yapamwamba anapasa moni muthu ogwila ganyuyi nati mulibwanji uncle muthuyi poyakha anati mmmmmm sizikuyenda mix maluzi ndilibe ndalama ndikumangopeza chakudya chalelo basi muthu uja anati oky Mulungu ndiwadongosolo sikulina zizayena ndipo anapita

Patapita masiku ochepa muthu uja adabwelaso anampasa moni moyo ulibwanji muthu uja anayakhaso zithu sizikuyenda mavuto okhaokha paliibe chabwino pazikopano chomwendikuona muthu olemela uja nati oky

Siku linaso anabwela nati moyo ulibwanji lelo ndipo iye anayakhaso chimozimozi nati mavuto boss bolaso kufa bwana uja anafusa nati

Kodi Mungalore munthu akupaseni 100 billion komaso nyumba yabwino ndi Galimoto 5 komaso ak*tengeleni ku UK 🇬🇧 kwa wiki imodzi koma pakatha mwezi umozi mufe kodi mungalole

Muthu unja anati ayi sindingalole bolaso ndizivutika chumachosecho ndichisiyaso aaa palibe chabwino

Bwanayi anati m'bale wanga zonse uzionazi nzachabe moyo ndiye uposa zonse pamene ukumana ndi mavuto lemekeza kumwamba chifukwa chamoyo

Taona mzako ine ndili ndigalimoto 10 zazikulu makapani 5 ndili ndindalama zambili koma ndili ndi nthenda ya cancer ya mmagazi moti ndikuchoka ku India 🇮🇳 kuchipatala komwe asimikiza k*ti mwezi uno siutha ndisanamwalile chumachanga chalephela kugula moyo uziyamika Mulungu chifukwa chamoyo

Ndikunena ndiwe iwe mmbale amene lelo ulibizy k*tchula za uphawi wako koma ukuiyiwala mphaso yamoyo

Kusayenda bwino kwa ziko uphawi mavuto asatiyiwalise k*ti Mulungu ak*tipasabe m'daliso wamoyo tiziyamika kumwamba nthawi zonse

banja limatha chuma chimatha ubale umatha zose zidzatha koma mau AMULUNGU adzakhala ku THAWI za THAWI

masali 103v1 lemekeza yohova MOYO wanga ndikusayiwala zokoma zose zimene amatichitila AMEN AMENIIIIII 🙏🏼🙏✍️

16/01/2025

*Kukhala molingana ndi maimvaimva a thupi ndi ulamulira wa kumdima*

Ndithudi kubvomeledza Yesu ndikumvera iye sichapafupi chifukwa ndi ambiri akufuna koma satana wawasenzetsa mtolo wa tchimo ndipo sangatulukemo popanda Ambuye kulowelerapo.

Mu 2 Akorinto 5:16-21

Molingana ndi malemba pa Aroma 8:1-17, kukhala ndi moyo wolamuliridwa ndi thupi ndiko kukhala ndi maganizo odana ndi Mulungu komanso moyo womusangalatsa Mulungu. Kukhala molingana ndi thupi kumabweretsa chilango cha imfa (Aroma 8:6, 13).

Kwa Paulo, zilakolako za thupi sizigwirizana konse ndi chipatso cha mzimu woyera mwa ife (Agalatiya 5:16-24). Mu Agalatiya 5-6, chipatso cha mzimu woyera ndicho chizindikiro chenicheni cha zochita za Mulungu za chilengedwe chatsopano mwa ife tikabadwanso mwatsopano — ndi mchitidwe wa k*tisintha ndi k*tiwombola komanso kuitana anthu onse ku moyo watsopano.

Pa 2 Akorinto 5:16, pamene Paulo akunena k*ti sakudziwanso aliyense “molingana ndi thupi,” Paulo akuvomerezanso k*ti moyo wake mwa Khristu ndi ntchito ya Mzimu Woyera mkati mwake (onani, mwachitsanzo, 2 Akorinto 3:5- 6; 4:13-15; 5:5).

Mulungu wamupulumutsa ku mphamvu ya thupi ndi kumuthandiza kuyenda molingana ndi Mzimu.
Chatsopano Chafika
Ntchito ya Mzimu ndi chitsimikizo chak*ti m'badwo watsopano wayamba (5:5).

Zatsopano ndi zakale zikuyimira maufumu omwe amasemphana kwambiri.

Ufumu wa Mulungu ndi m’badwo watsopano, ndipo unakhazikitsidwa ndi moyo, imfa, ndi chiukitsitso cha Yesu.

Ufumu wa kumdima ndi ulamuliro wa mphamvu yak*thupi yomwe yimadana ndi za Mulungu mwa iwo omwe mphamvuyo siyinafe.

Ambuye atithandize kuima p a chikhulupiriro cha moyo watsopano mwa Yesu Khrisitu ndikuyenda mogonjera iye, osabweleranso kunjira ya ku mdima wa imfa.

Sungani chipulumutso cha Khrisitu nthawi zonse. Iyi yikhale nyale ya moyo wanu wosatha.

Ambuye atithandize ndithu 🙌

15/01/2025

KODI INU MUNGAPANGE IZI👇🏾

Panali mnyamata wina yemwe anayimbila 4n mzake kumuuza k*ti "mai anga akudwala komano ineyo ndilibe ndalama yokagulila mankhwala omwe akufunikilawo,kodi ungandibwerekeko ndalamayo? "

Mzake uja anayankha mwachidure nati "chabwino mzanga ndakumva,undiyimbireso panopa ndili m'mapemphero".

Ofuna thandizoyu atayimbaso,padapezeka k*ti 4n yanzake uja yazimitsidwa.

Apa mnyamatayu anayesetsa kufuna funa anzake ena oti amubwereke ndalamayo,koma sanapezeke.

Atatopa nkufuna omuthandiza,anabwelela kunyumba ndipo atalowa mnyumba anapeza mulu wa mankhwala a mitundu yonse omwe amafunikila aja ali pambari pa pilo wa mai ake odwalawo,amaiwo atagona.

Mnyamatayu atafusa mng'ono wake za komwe kwachoka mankhwalawa,mng'ono wake uja anayankha k*ti mzako uja ndamene anabwela kudzatenga pepala la mankhawala omwe amafunikawa ndipo kenaka wabweretsa mankhwalawa moti mwangosemphana akupita pompano.

Ndi misonzi m'maso mwake,mnyamata uja adasekelela ndipo kenaka adauyamba omulondola mzake uja.Atapezana naye adamufusa k*ti "ayise unali k*ti?ndakhala ndikukuyimbila koma 4n yako inathimitsidwa"

Mzake uja atamva fusoli adayankha nati "4n ndagulitsa ndipo ndalamayo ndakagula mankhwala a mai ako aja"

đź“ŚANZATHU PA MAVUTO NDE ANZATHU ENIENI
-------------------------------------------------------------
Ndifusanso...Kodi inuyo mungapange zimenezi?

Mukhare ndi tsiku labwino pomwe mukuganizila za nkhaniyi,Ambuye akudalitseni🙏🏾.

09/01/2025

Big shout out to my newest top fans! Belina Phili, Patuma Yakin, Christina Wa Mike Banda, Rosalia Kathumba

MZIMAYI YEMWE WAKANA K500,000 YA TRIEPHORNIA MPINGANJIRA WATI SANGALOLE KUPITA KU GEHENA CHIFUKWA CHA CHUMA CHA DZIKO LA...
03/01/2025

MZIMAYI YEMWE WAKANA K500,000 YA TRIEPHORNIA MPINGANJIRA WATI SANGALOLE KUPITA KU GEHENA CHIFUKWA CHA CHUMA CHA DZIKO LAPANSI

Mzimayi wina ogulitsa tomato yemwe wakana kulandila ndalama zokwana K500,000 zomwe mayi, Triephornia Mpinganjira amamupasa k*ti atukulire business yake wati sangalole kukaphya ku gehena chifukwa chofuna chuma cha dziko lapansi.

Poyankhula ndi antolankhani, mayiyu wati anakana kulandila ndalama zochokela kwa mayi Mpinganjira kaamba koti sakudziwa bwino momwe mayiwa anapezela chuma chawo komanso zolinga zawo powapasa ndalamazo.

Iwo adati nthawi zina satana amathanso kumupasa munthu ndalama ncholinga choti amusocholetse, amuphe kapena kumutengela kuchiwongeko kotelo iwo adachiwona chofunikila kwambili kuwukaka m'dalitsowu ncholinga choti azakakumane ndi Mulungu masiku awo okhalira padziko lapansi akazatha

Mayiwa apempha azimayi anzawo k*ti azilimbikila ntchito osati kudalira zinthu za ulele zochokela kwa anthu osawadziwa ponena k*ti zambili zimabwela ndimavuto, minyama matsauso komanso chiwonongeko. Iwo atinso kuyika Mulungu patsogolo muchina chilichonse nkwabwino kaamba koti kumathandiza munthu kupewa mayesero a satana akafika.

28/12/2024

MWAGWIRA CHIYANI MMANJA MWANU.....
Mkulu wina yemwe ankadusa munjira ina anapeza mzimai atavula nsapato zake, kwinaku akumangila nsalu yake molimba, miyala yake itatu ili poteropo...
Mkuluyo anali odabwa ndizomwe amachita mai yo ndipo anamufunsa:

🤷‍♂️"KODI MAYI CHIKUCHITIKA NDI CHIYANI"?
Mzimai uja mosasamala kwambiri anati,
🙅‍♀️"ohoooo!!! Kodi k*tero simukuziwa k*t nyumba yapatsogoloyo pali agalu olusa, ineyo apapa k*tero ndamangila kale nsalu yanga, nsapato zangaz zikhala manja, lero agalu amenewa adziwanso, ndikakawandikira, nkangowagenda kenako ndikathamange chiliwiro basi ndiduse"...
Mkulu uja anamuyang'ana mzimai uja ndipo anamuuza k*t;
🤔"MAI INU MULI NDI TSOKA, NDIPONSO MWINA MUTU WANU SUKUGWIRA, MIYALA MWATENGAYI, MUTAKHALA MWAMUPHONYA GALUYO, MUNGATHAMANGISANE NAYE? MMENE GALU AMATHANGILA MUNGACHITE NAYE MPIKISANO"?
...
Mzimai anangot zyoliii ndipo mkulu uja analowa pakatchire nafuna NDODO yabwino yamphamvu namupasa mai uja, ndipo anamuuza k*t avale nsapato zake...
Anamutsimikizira k*t choyamba akhulupire k*t MTENGO WAMUPATSAWO UMUTHANDIZA, CHIFUKWA KAKHULUPIRIRA, SANGAUTAYE ANGAKHALE AGALU ATACHITA UKALI CHOTANI, AZADUTSA MOSAVUTA CHIFUKWA SAZAFIKA NAYE PAFUPI..
Mzimai anadutsa mosavuta, agalu ankangochita ukali osafika naye pafupi.....
M'bale kunja kuno kuli agalu, kulimbana nawo wekha, popanda chilichonse Mmanja mwako, sungapambane...KODI MWAGWIRA CHIYANI MMANJA MWANU?
Okondedwa k*tero satana pa inu nokha simungapange nae mpikitsano, satana ali ndi mphamvu, ndipo ndiiye akulamula dziko la pansi YOHANE 14 VS 30 .
Anthu lero atenga miyala nkuika mmanja, ati kufuna kulimbana ndi mkuru wa dziko lapansi, Miyala imene itatitaika tizasowa chozitetedzera, tikudalira nyanga, ziwanda pofuna kulimbana ndi mkuru wadziko lapansi... l MUkatenga miyala nkuika manja mwanu kuchekera, k*tsilika nyumba k*tsilika business, nkumat Mukulimbana nae, nkumati mwathana nae ndiye mwasaka njira yolakwika, chifukwa simukudziwa k*t komwe mwakatenga zimenezo ndi kwa bambo wake wa iyeyo satana, akupasani bwanji zogonjesera ufumu wake, chabwino nanga zitakhala k*t zomwe akupasanizo zatha ntchito, mungalimbe polimbana ndi mfiti inu?..
YOHANE 14 VS 6...YESU anati, INE NDINE NJIRA CHOONADI NDI MOYO, PALIBE MUNTHU ADZA KWA ATATE KOMA MWAINE...
Okondedwa ndi Yesu yekha ndiye Njira yabwino yogonjesera oipa... Tengani Yesu akhale NDODO yanu..akhale mumtimamo
Mkulu uja anamuuza mai uja k*t choyamba akuyenera kukhulupira k*t ndodo ija imuthandiza ndipo izamuthandizad pamavuto sangaitaye, ifenso tiyen tikhulupirire Yesu yemwe ali mumitima yathu ndipo tikatero angakhale zitavuta sitingakagwadenso kwa milungu yakunja, sik*t pamene uli ndi Yesu agalu samachita ukali ai, sik*t satana asiya kulimbana nawe ai, sik*t mayesero alekeka ai..., koma baibulo lik*ti Mulungu sazalola k*t tizayesedwe moposera msinkhu wathu, azaonesesa k*t waika adani onse kunsi kwamapaz athu, EXODUS 14 VS 14 azatigwirira nkhondo tili chete..
Tiyeni tisanyengeke ndi nkhalidwe wina uliwonse odza ndi mphamvu ya oipayo, angakhale zitakoma chotani, mutalemera chotani koma kumbukiran k*t slogan ya satana ndi KUPHA..KUBA .. NDI KUONONGA...CHISANGALALO CHILICHONSE POPANDA JESUS IS EQUAL TO GAHENA....
AMBUYE AKUDALITSENI NDIPO MUKHALE NDI TSIKU LABWINO ..

28/12/2024

*PAKHONDE LANU PAMAONETSERA CHANI ZA MKATI MWANU*

_Tsiku lina zinandipatsa chidwi kuwona pakhonde pa nyumba ya wogulitsa chimanga, chili bweee! Kutaika taika._

_"Ndinadzilankhulira k*ti uku sikuononga chakudya uku!!"_

_Tsiku lina ndinaonanso pa khonde pa butchery, pataikira tima piece tanyama kugwera pansi. Ogulitsa kumangotisiya osatola._

_"Ine aaaah! koma awa kumataya nyama zoona?"_

_Ndiyeno, tsiku lina mshop mwathu sugar anataika, ndinatenga tsache mkusesera paja._

_Apa mpamene mutu wanga unasauka ndimaganizo. Ndinazindikira k*ti zomwe zimataikira pakhonde zimaonetsera zomwe zili mkatimo._

_Musadzadabwe kumuona munthu ak*tukwana. Mudzangodziwa k*ti watayako zochepa mwa zomwe zili mkati mwake._
_Kumuona mkazi ataminula mopanda manyazi, kapena mwamuna atakhwefula, dziwani k*ti mkati mwake adavula kale._

_Zimene timachita kaya kuyankhula zimaonetsera yemwe ali mkati mwathu._ _Mudzamuona inu munthu wokonda kwambiri mpira, amachita kuloweza maina onse ama player._
_Woopa Mulungu nayenso mudzamudziwa ndimalankhulidwe ake aulemu, ndipo pakamwa pake sipatuluka chichewa chovunda. Mawu a Mulungu k*ti,_
*_"Koma zak*turuka m'kamwa zichokera mumtima"._*
*MATTHEW 15:18*

_Pakamwa pathu ndipakhonde, zimene zimatuluka ndizomwe zili mkati._
_Tikakonza mkati mwathu, zotuluka pakamwa zidzakhalanso zabwino._
_Sizisowekeranso kufunsa, zimadziwika zokha k*ti awa mkati mwawo muli chonchi, awanso muli chonchi malingana ndi momwe ife timayankhulira ndi kuchitira zinthu._

_Ambuye wodziwa kukonza atithandize kukonza mkati mwathu k*ti pakhonde padzachitire umboni._
*Amen.*

Address

Ekwendeni
Lilongwe

Opening Hours

09:00 - 17:00

Telephone

+265881367538

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Victor Creatives posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share