Kasungu Community RADIO

  • Home
  • Kasungu Community RADIO

Kasungu Community RADIO Our VISION is to be the most VALUED, TRUSTED and VIBRANT radio station that inspires communities

Wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino Dr. Michael Usi ali nawo pa mwambo woyika m'manda thupi la malemu Kester Kaphaizi,...
08/03/2025

Wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino Dr. Michael Usi ali nawo pa mwambo woyika m'manda thupi la malemu Kester Kaphaizi, kumudzi kwawo kwa Kaphaizi kwa mfumu yaikulu Kaphaizi m'boma la Kasungu.

Kufikira imfa, a Kaphaizi anali kazembe wadziko lino ku Ethiopia komanso nthumwi yadziko lino ku mabungwe a African Union ndi United Nations Economic Commission for Africa, ndipo anakhalaponso mlembi wamkulu m'maunduna a maboma ang'ono ndi mphamvu zamagetsi.

A Kaphaizi anamwalira pa 3 mwezi uno ali ndi zaka 69 m'dziko la India komwe amkakalandira thandizo lamankhwala atavutika ndi khansa ndipo asiya mkazi ndi ana anayi komanso zidzukulu zitatu.




Mverani KCR pa 107.6 MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Alenje a boma ku nkhalango ya Kasungu agwira a Gibson Chatambalala azaka 48 womwe anawapeza akugulitsa nyama ya Njati yo...
08/03/2025

Alenje a boma ku nkhalango ya Kasungu agwira a Gibson Chatambalala azaka 48 womwe anawapeza akugulitsa nyama ya Njati yomwe akuwaganizira kuti anapha m'nkhalangoyi.

Mkulu wa nkhalangoyi a Ndaona Kumanga watsimikiza za nkhaniyi ponena kuti kugwidwa uku a Chatambalala ndi kwa chitatu kaamba kosaka nyama m'nkhalangoyi.

A Chatambalala womwe ndi a m'mudzi mwa Chikwiyo kwa Chulu, mu 2022 bwalo la milandu linawagamula pa mulandu wopha nyama kuti akakhale ku ndende kwa zaka 7 komwe ati anangokhalako zaka ziwiri zokha.

Enanso mwa anthu omwe awagwira powaganizira kuti amasaka m'nkhalangoyi pa chipikisheni chomwe alenjewo anachita ndi a Chuluchandiwo Phiri, 68, a m'mudzi mwa Chioza ndi a Charity Banda, 34, a m'mudzi mwa Chikwiyo, onse m'dera la mfumu yaikuku Chulu.

Wolemba Topson Banda




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu kudzera 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

M'boma la Kasungu, asilamu awalangiza kuti apewe mchitidwe woyipa maka m'nyengo ino yomwe akusala.Sheik Ishmael Abdul pa...
07/03/2025

M'boma la Kasungu, asilamu awalangiza kuti apewe mchitidwe woyipa maka m'nyengo ino yomwe akusala.

Sheik Ishmael Abdul pa mzikiti wa Kasungu Central wati anthu ena amayiwala chifukwa chomwe akusalira maka nthawi ya madzulo akamasula.

Sheik Abdul wati kusala sikutanthauza kuti ukamasula nde kuti munthu umasuke, kuchita zinthu zoyipa mudzina la kudzipepesa chifukwa cha maola omwe wakhala ukusala.

Malinga ndi Shaik Abdul, ino sinthawi yoti asilamu azikhala m'magulu aziwawa ndi kuchita zinthu zoyipa monga chigololo koma m'malo mwake akuyenera kusunga chiyero.

Asilamu anayamba kusala pa 2 mwezi uno ndipo akhala akusala kwa masiku makumi atatu.

Wolemba Aisha Mkwamba




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

(M'zithunzi: Ena mwa asilamu m'bomali)

Vuto lamadzi ladandaulitsa ophunzira pa sukulu yosula aphunzitsi ya Kasungu TTC.Malinga ndi zomwe tapeza, bungwe la Cent...
06/03/2025

Vuto lamadzi ladandaulitsa ophunzira pa sukulu yosula aphunzitsi ya Kasungu TTC.

Malinga ndi zomwe tapeza, bungwe la Central Region Water Board linadula madzi pasukulupo chifukwa cha ngongole ya mabilu amadzi pafupifupi K100 million.

Mmodzi mwa ophunzira omwe anati tisamutchule dzina wati akumakanganirana madzi pa mjigo womwe uli pa sukulupo.

Iye wati vutoli likuchititsa kuti azichedwa m'kalasi, ndipo aphunzitsi akumawalanga ponena kuti akuyenera kumatunga madzi usiku.

Koma akuluakulu pa sukulupo anati tiyankhule ndi unduna wa zamaphunziro ndipo mneneri mu undunawu Mphatso Nkuonera wati ayankha akafufuza bwino za nkhaniyi.

Bungweli ladulanso madzi pa chipatala chachikulu cha Kasungu kaamba ka ngongole ya mabilu amadzi. Wofalitsa nkhani za umoyo a Catherine Yoweli watsimikiza.

M'mbuyomu, akuluakulu a zaumoyo m'bomali ananenapo kuti chipatalachi chikuvutika kubweza ngongole ya madzi yoposa K100 million ku bungweli.

Wolemba Davie Banda




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatuvu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets ili ndi masewero anayi omwe isewere popimana mphamvu ndi ma timu ena omwe amasewera mu lig...
05/03/2025

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets ili ndi masewero anayi omwe isewere popimana mphamvu ndi ma timu ena omwe amasewera mu ligi ya TNM, ligiyi isadayambe chaka chino.

Izi ndi malinga ndi tsamba la mchezo la Facebook la timuyi.

Bullets yomwe idakhala yachitatu mu ligi ya TNM chaka chatha isewera ndi Kamuzu Barracks pa 16 March pa bwalo la Champion ku Mponela m'boma la Dowa.

Ikatero, timuyi ikuyenera kutenga nawo gawo mu mpikisano wa Sapitwa pa bwalo la Mulanje komweso kudzakhale ma timu ena monga Creck Sporting, Mighty Tigers komaso Ekhaya pa 22 ndi pa 23 mwezi uno.

Ndipo pa ulendo womaliza kukozekera chaka cha tsopanaochi cha zamasewero pansi pa m'phudzitsi wawo Peter Mponda timuyi idzamaliza zokozekela zake ndi timu ya Blue Eagles pa bwalo la Aubrey Dimba ku Mchinji pa 31 mwezi uno.

Wolemba Lucky Millias




Mverani KCR pa 107.6MHz Kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Akuluakulu a khonsolo ya boma la Kasungu avomereza ntchito yomanga malo ophikiramo chakudya (Kitchens) ogwiritsa ntchito...
05/03/2025

Akuluakulu a khonsolo ya boma la Kasungu avomereza ntchito yomanga malo ophikiramo chakudya (Kitchens) ogwiritsa ntchito njira zosaononga chilengwe pophika, m'sukulu za pulaimale 47 m'bomali.

Bungwe la World Food Programme (WFP) ndilo ligwire ntchitoyi m'sukuluzi, zomwe limazithandiza ndi chakudya monga phala lomwe ophunzira amalandira.

Pofotokozera akuluakulu a khonsoloyi pa mkumano wa DEC lero, akuluakulu a bungweli ati amanganso zipinda zosungiramo katundu m'sukuluzi.

Mulangizi wamkulu woona za chisamaliro cha anthu m'bomali Victor Williams Nyirenda wati mwazina akuyembekeza kuti ntchitoyi ilimbikitsanso ukhondo mmalo omwe amaphikiramo phala m'sukuluzi.

Bungweli linayeselera kale njira zosaononga chilengwe pophika posadalira khuni koma kugwiritsa ntchito magetsi a dzuwa m'sukulu za Kasamba, Kaunde ndi Katuta, kotero ndi chifukwa chake likufuna kumanga malowa ndi thandizo lochokera ku NORAD.

Wolemba Samson Baza




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatuvu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Bungwe la Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA) lati ndi lokhutira ndi momwe ntchito yophunzitsa ophunzira ...
04/03/2025

Bungwe la Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA) lati ndi lokhutira ndi momwe ntchito yophunzitsa ophunzira a m'sukulu za pulaimale chiyankhulo cha manja ikuyendera m'boma la Kasungu.

Rachael Chadowa, kuchokera ku nthambi ya Universal Service Fund pansi pa bungweli ndiye wanena izi lero pomwe amayendera ntchito za phunziroli pa sukulu ya Demonstration yomwe ili ku Kasungu TTC.

A Chadowa ati anakhanzikitsa phunziroli m'sukuluzi za m'dziko lino ndi cholinga chakuti pazikhala kulumikizana mosavuta pakati pa ophunzira omwe ali ndi ulumali osayankhula ndi kumva komanso omwe alibe ulumaliwu.

Mphunzitsi yemwe akuyang'anira phunziroli pa sukulupo a Mercy Mkosi wati pakadali pano ana ochuluka ayamba kudziwa chiyankhulochi.

Komabe a Mkosi apempha bungweli kuti liwathandize ndi makina a ‘Projector' kuti ophunzira azitha kuona mosavuta pomwe akuphunzira chiyankhulochi.

Wolemba Davie Banda




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

M'boma la Kasungu ndi m'manisipalite ya bomali, bungwe la MEC liyamba kugwira ntchito yosintha malo oponyera voti kwa an...
04/03/2025

M'boma la Kasungu ndi m'manisipalite ya bomali, bungwe la MEC liyamba kugwira ntchito yosintha malo oponyera voti kwa anthu omwe akufuna kusintha kuyambira mawa mpaka pa 7 mwezi uno.

Ili ndi gawo lachiwiri la ntchitoyi ndipo bungweli likhala ligwiranso m'maboma a Rumphi, Nkhata Bay, Likoma, Dowa, Mchinji, Ntcheu, Blantyre, Blantyre City, Zomba, Zomba City, Thyolo ndi Luchenza Manisipalite.

Mkulu wofalitsa nkhani ku bungweli a Sangwani mwafulirwa watsimikiza za nkhaniyi.

A Sangwani ati anthu omwe akufuna kusintha malo oponyera voti, akuyenera kupita kumalo omwe akufuna kudzaponyera voti kuti akawathandize.

Malinga ndi a Mwafulirwa, bungweli likatsiriza ntchitoyi, pali yemwe adzaloledwe kusintha malo oponyera voti, kotero anthu omwe akufuna kusintha akuyenera kugwiritsa ntchito mwayiwu.

Anthu omwe anataya chiphanso cha unzika ndi chovotera nawo ati ali mwayi oti atha kusintha malo oponyera voti, komabe palibe yemwe adzaloledwe kusintha m'malo mwa mnzake.

Nzika za dziko lino zikuyembekezeka kusankha mtsogoleri wadziko, aphungu ndi ma khansala pa 16 September chaka chino.




Mverani KCR pa 107.6MHz Kapena pa utatuvu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Noel Mkubwi yemwe akufuna kudzapikisana nawo pa mpando wa phungu wa nyumba ya malamulo mu dera la manisipalite ya Kasung...
03/03/2025

Noel Mkubwi yemwe akufuna kudzapikisana nawo pa mpando wa phungu wa nyumba ya malamulo mu dera la manisipalite ya Kasungu wakhazikitsa ntchito yothandiza achinyamata kuphunzira luso la ntchito za manja, pofuna kutukula miyoyo yawo pachuma.

Pakadali pano, achinyamata khumi ndi awiri m'manisipaliteyi ayambe kale kupindula ndipo ali pa sukulu yosula achinyamata luso la ntchito za manja ya Kasungu.

A Mkubwi anena izi lero pa sukulu ya Boma CDSS m'manisipaliteyi pomwe anachititsa msonkhano womwe unapereka mwayi kwa achinyamata kuti aonetse luso lawo.

M'modzi mwa achinyamata opindulawo, Chilungamo Phiri yemwe akuphunzira kuwotchelera wayamikira a Mkubwi pomuthandiza ndipo wati wayamba kale kudyelera lusolo.

Wolemba Tadala Hudson Njelesa.




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Mkulu wa chipinda chokonza nkhani za masewero ku wailesi ya Kasungu, Lucky Millias amusankha ngati mtolankhani yemwe akh...
03/03/2025

Mkulu wa chipinda chokonza nkhani za masewero ku wailesi ya Kasungu, Lucky Millias amusankha ngati mtolankhani yemwe akhale akufalitsa nawo nkhani za masewero okankha chikopa m'chigawo chapakati.

Bungwe loyendetsa masewerowa m'chigawochi la Central Region Football Association (CRFA) lalengeza kuti lasankha gulu la atolankhaniwa, lomwe ligwire ntchitoyi chaka chino ndipo mulinso atolankhani monga Sam Banda, John Palichesi ndi Frank Kalilombe.

Kupatula kukonza nkhani, Lucky amaulutsanso ma pulogilamu a zamasewero pa wailesi ya Kasungu ndipo amadziwika ndi dzina lakuti ‘Mphangala pa Chikopa.'




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Nduna ya zaumoyo a Khumbize Kandodo Chiponda yati boma liri ndi malingaliro okuza chipatala chaching'ono cha Kasalika m'...
03/03/2025

Nduna ya zaumoyo a Khumbize Kandodo Chiponda yati boma liri ndi malingaliro okuza chipatala chaching'ono cha Kasalika m'manisipalite ya Kasungu kukhala chipatala chachikulu chakumudzi (Kasilika Rural Hospital).

Ndunayi yanena izi lero pa mkumano wa akuluakuku a khonsolo ya boma la Kasungu ovomereza ndondomeko ya zachuma ya 2025-26.

A Kandodo Chiponda ati chipatala cha Kasalika chitha kuthandiza kuchepetsa kuthithikana pa chipatala chachikulu cha Kasungu, chomcho nkofunika kuti chipatala cha Kasalikachi achikuze.

Khonsolo ya boma la Kasungu, ikuyembekezekanso kumanga chipinda chogonamo odwazika odwala pa chipatala chachikulu cha Kasungu, chomwe anthu akhala akuchilakalaka.

Khonsoloyi ikuyembekezeka kulandira thandizo lomangira chipindachi, kuchokera mu thumba la CDF ndipo phungu aliyense m'bomali akuyenera kusonkha K20 million kuchokera mu CDF.

Wolemba Topson Banda




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3
(M'zithunzi: nduna kuyendera malo omwe odwazika odwala akukhala pa chipatala Cha Kasungu)

khonsolo ya boma la Kasungu lero yavomereza ndondomeko ya zachuma (Budget) ya chaka cha 2025-26 yomwe yanyamula ndalama ...
03/03/2025

khonsolo ya boma la Kasungu lero yavomereza ndondomeko ya zachuma (Budget) ya chaka cha 2025-26 yomwe yanyamula ndalama zokwana K56 billion.

Ndalamazi zikuyembekezeka kuchokera ku boma (Central Government Transfers), misonkho ndi abwenzi ogwira nawo ntchito pachitukuko (Development Partners' Budget) monga World Bank, European Union (EU) World Vision ndi Flanders.

Mwa ntchito zina zachitukuko, khonsoloyi ikuyembekezeka kutsiriza msika wa Chamama ndi Simulemba, kumanga chipinda chogonamo odwazika odwala pa chipatala chachikulu cha Kasungu, zipinda zochiliramo amayi pa zipatala zing'onozing'ono za Chamama ndi Livwezi, TDC ya Mthawira Zone kwa T/A Mdunga ndi damu la Maluvenji kwa Simulemba.

Wolemba Topson Banda




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatuvu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Abambo awiri ali m'chitokosi cha apolisi ku Kasungu atawapeza ndi njinga zamoto zinayi zomwe akuwaganizira kuti anachita...
02/03/2025

Abambo awiri ali m'chitokosi cha apolisi ku Kasungu atawapeza ndi njinga zamoto zinayi zomwe akuwaganizira kuti anachita kuba.

Mneneri wa apolisi m'bomali a Joseph Kachikho wati izi zikudza kutsatira kafukufuku yemwe apolisi akhala akuchita m'bomali kaamba ka kukula kwa mchitidwe wakuba njinga zamoto.

A Kachikho ati awiriwa ndi amodzi mwa anthu omwe akumachita hayala njinga zamoto za kabaza mwadala kenako ndi kuvulaza kapena kupha kumene oyendetsa ndi kuba njingazo.

Pakadali pano eni njingazo sanadziwike ndipo owaganizirawo akuyembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu.

Posachedwapa akuluakulu oyendetsa njinga zamoto za kabaza m'tauni ya Kasungu anadandaula za kukula kwa mchitidwewu omwe ati ukuyika miyoyo yawo pachiopsyezo.

Awiriwo ndi Frackson Funsani, 33, wa m'mudzi mwa Phiko T/A Chakhadza ku Dowa ndi a Fanuel Yesaih, 36, a ku Camel, kwa mfumu yandodo Kaomba ku Kasungu.




Mverani KCR pa 107.MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Apolisi ku Kasungu amanga abambo awiri powaganizira kuti akhala akuopsyeza anthu anayi m'bomali kuti iwo ndi mbava zoopy...
02/03/2025

Apolisi ku Kasungu amanga abambo awiri powaganizira kuti akhala akuopsyeza anthu anayi m'bomali kuti iwo ndi mbava zoopysa zoba ndi mfuti pomawatumizira mauthenga a palamya.

Anthuwa omwe ndi a Bright Mgemezulu azaka 40, ndi a Ephron Nyirenda azaka 61 akhala akuopsyeza anthuwa kuti awapha akachita chibwana kuyambira m'chaka cha 2023.

Kenako awiriwa, pogwiritsa ntchito nambala zina za lamya, anayamba kuvutitsanso anthuwa kuti iwo ndi asing'anga omwe akukhala ku Mozambique koma a Nyirenda ndi nthumwi yawo kuno ku Kasungu ndipo akudziwa za mavuto awo, kotero atha kuwathandiza.

Wichiwiri kwa mneneri wa apolisi m'bomali a Miracle Hauli wati:

“ Abambo omwe tawamangawa akhala akuuza anthu anayiwo kuti azikasiya ndalama pa mntengo omwe uli m'munda mwa a Nyirenda pomwenso ati amapezapo mankhwala azitsamba."

Anthuwa ataona kuti zisikuyenda anatsina khutu apolisi omwe atachita kafukufuku wawo, amanga abambo awiriwo omwenso ati avomera za nkhaniyi ndipo awapeza ndi ma simukhadi 12.

A Mgemezulu ndi a m'mudzi mwa Nyezani pomwe a Nyirenda ndi a m'mudzi mwa Ndacha, onse kwa mfumu yaikuku Chisinga m'bomali.




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu Kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Achinyamata mu mpingo wa CCAP Nkhoma Synod pansi pa Presbytery ya Chamwabvi ku Kasungu, awalimbikitsa kuti pomwe akutumi...
01/03/2025

Achinyamata mu mpingo wa CCAP Nkhoma Synod pansi pa Presbytery ya Chamwabvi ku Kasungu, awalimbikitsa kuti pomwe akutumikira Mulungu, aziyesetsanso kutakataka kuti miyoyo yawo itukuke.

Yemwe akufuna kudzapikisana nawo pa mpando wa phungu mu dera la ku m'mawa kwa bomali Alex Nkhoma wanena izi lero pa mwambo wobzyala mitengo womwe achinyamatawa anakonza pa Livwezi CCAP kwa mfumu ya ndodo Wimbe.

A Nkhoma ati achinyamata akuyenera kukhala ochilimika ndi kumatenga nawo gawo pa ntchito zomwe boma likulimbikitsa monga kusamalira za chilengedwe, ngati momwe achitira lero.

Commissioner wa achinyamata mu presbytery-yi Rv. Gilbert Isaac Davies Njobvuyalema wati achita chotheka kulimbikitsa achinyamatawa kubzyala mitengo komanso kumayisamalira.

Pakadali pano khonsolo ya bomali ili mu nyengo yobzyala mitengo ndipo chaka chino, pali chiyerekezo chobzyala mitengo 3 million.




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Anthu achikulire oposa 150 kwa mfumu yaikulu Dambe ku Mchinji, akuyembekezeka kupumulako ku ululu wa njala kwa masiku an...
01/03/2025

Anthu achikulire oposa 150 kwa mfumu yaikulu Dambe ku Mchinji, akuyembekezeka kupumulako ku ululu wa njala kwa masiku angapo tsopano.

Izi zikudza kutsatira thandizo la chimanga lomwe wochita malonda Atupere Makwinja wa kwa Santhe ku Kasungu wapereka kwa achikulirewo lero.

A gogo a Dambe ayamika a Makwinja kaamba ka thandizolo ponena kuti pakadali pano njala yafika pachimake, maka mma'dera akumidzi.

Mbali yawo, a Makwinja ati ndi khumbo lawo kuthandiza anthu achikulire omwe ndi osowa, ponena kuti Mulungu amadalitsa opereka.

Anthuwa, aliyense walandira 20kg ya chimanga ndi soya pieces, mwazina.

Wolemba Pofera Chinkhwasale -Santhe




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatavu Kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Bungwe la AIDS Interfaith ku Kasungu lapempha anthu m'bomali kuti achilimike kubzyala mitengo ndi kumayisamalira.Wapampa...
28/02/2025

Bungwe la AIDS Interfaith ku Kasungu lapempha anthu m'bomali kuti achilimike kubzyala mitengo ndi kumayisamalira.

Wapampando wa bungweli Henry Lunda wanena izi lero pa mwambo wobzyala mitengo pa sukulu ya pulaimale ya Mtsita m'dera la mfumu ya ndodo Mwase.

A Lungu ati pakadali pano dziko lino likukumana ndi mavuto akusintha kwanyengo monga mphepo zankuntho ndi ng'amba, zinthu zomwe zikuchulukira kaamba ka kusakazika kwa chilengedwe.

Wapampando wa komiti ya PTA pa sukulupo a Jessi Phiri wayamika bungweli kaamba ka ntchitoyi, ponena kuti sukuluyi kukhala yatsopano, pakufunika mitengo.

A Phiri ati asamalira mitengoyi komanso kupitilira kubzyala ina.

Wolemba Sellaphine Banda




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatuvu kudzera pa 👇🏾

Anthu ali ndi chimwemwe m'mudzi mwa Kampaliro, T/A Chisemphere kumpoto kwa boma la Kasungu pomwe achiwiri kwa nduna yoon...
28/02/2025

Anthu ali ndi chimwemwe m'mudzi mwa Kampaliro, T/A Chisemphere kumpoto kwa boma la Kasungu pomwe achiwiri kwa nduna yoona za maboma ang'ono, umodzi ndi chikhalidwe Joyce Chitsulo akuyendera sukulu yatsopano ya Chikaka.

Ndi pa 10 mwezi uno pomwe khonsolo ya bomali idapereka ntchito yomanga sukuluyi kwa kontirakita Bonongwe Building Constructions koma pofika lero mdadada wa zipinda ziwiri ndi ofesi ya aphunzitsi komanso zimbudzi zatha kale ndipo ngakhale mjigo wakumbidwa kale.

Nkale lonse, m'derali munalibe sukulu ndipo ana akhala akuyenda mtunda oposa makilomita asanu kuti akafike ku sukulu zozungulira, zomwe zimakolezera kusiyira sukulu panjira.

Khonsolo ya bomali igwiritsa ntchito ndalama yoposa K200 million pomanga sukuluyi.

Ndalamazi ndi za m'thumba la Performance Based Grant (PBG) pansi pa ntchito za Governance to Enable Service Delivery (GESD), lomwe chuma chake chimachokera ku World Bank kudzera ku bungwe la NLGFC.

Lero a Chitsulo ayendera zitukuko zosiyanasiyana m'bomali.

Wolemba Topson Banda




Mverani KCR pa 107.6MHz kapena pa utatuvu kudzera pa 👇🏾

https://live.netradio.pro/listen/kcr/radio.mp3

Address


Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Kasungu Community RADIO posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Kasungu Community RADIO:

Videos

Shortcuts

  • Address
  • Telephone
  • Alerts
  • Contact The Business
  • Videos
  • Claim ownership or report listing
  • Want your business to be the top-listed Media Company?

Share